Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • bi12 tsamba 1949-1950
  • 10 Yesu, Wonga Mulungu; Waumulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • 10 Yesu, Wonga Mulungu; Waumulungu
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
10 Yesu, Wonga Mulungu; Waumulungu

10 Yesu, Wonga Mulungu; Waumulungu

Yoh 1:1—“komanso Mawuyo anali mulungu (wonga Mulungu; waumulungu)”

Chigiriki, καὶ θεὸς ἦν ὁ λόγος (kai the·osʹ en ho loʹgos)

1808

“ndipo mawuyo anali mulungu”

The New Testament, in An Improved Version, Upon the Basis of Archbishop Newcome’s New Translation: With a Corrected Text, London.

1864

“ndipo mulungu anali Mawu”

The Emphatic Diaglott (J21, kuwerenga motsatira Chigiriki), lomasuliridwa ndi Benjamin Wilson, New York ndi London.

1879

“ndipo Mawu ameneyu anali mulungu”a

La Sainte Bible, Segond-Oltramare, Geneva ndi Paris.

1928

“ndipo Mawu ameneyu anali waumulungu”b

La Bible du Centenaire, Société Biblique de Paris.

1935

“ndipo Mawu ameneyu anali waumulungu”

The Bible—An American Translation, lomasuliridwa ndi J. M. P. Smith ndi E. J. Goodspeed, Chicago.

1950

“komanso Mawuyo anali mulungu”

Baibulo la Dziko Latsopano Lomasulira Malemba Achigiriki Achikhristu, Brooklyn.

1975

“ndipo mulungu (kapena kuti, waumulungu) anali Mawu”c

Das Evangelium nach Johannes, lomasuliridwa ndi Siegfried Schulz, Göttingen, Germany.

1978

“ndipo wonga Mulungu anali Logosi”d

Das Evangelium nach Johannes, lomasuliridwa ndi Johannes Schneider, Berlin.

1979

“ndipo mulungu anali Logosi”e

Das Evangelium nach Johannes, lomasuliridwa ndi Jürgen Becker, Würzburg, Germany.

Mabaibulo amenewa a Chingelezi, Chifalansa, ndi Chijeremani, amagwiritsa ntchito mawu akuti “mulungu,” “waumulungu” kapena “wonga Mulungu,” chifukwa chakuti mawu achigiriki akuti the·osʹ (θεός) analembedwa opanda mawu akuti ho. Koma pamawu akuti “ndipo Mawuyo anali ndi Mulungu,” “Mulungu” amene Mawuyo, kapena Logosi, anali naye pa chiyambipo, akutchulidwa pano ndi mawu achigiriki akuti ὁ θεός, kutanthauza the·osʹ wokhala ndi ho. M’Chigiriki choyambirira, kalembedwe kotere kamasonyeza kuti munthuyo ndani, pamene the·osʹ wopanda ho amasonyeza khalidwe la munthuyo. Choncho, mawu a Yohane akuti Mawuyo, kapena Logosi, anali “mulungu,” kapena “waumulungu,” kapenanso “wonga Mulungu,” sakutanthauza kuti iye anali Mulungu weniweniyo amene iye anali naye. Amangosonyeza khalidwe la Mawuyo, kapena Logosi, koma sakunena kuti iyeyo ndiye Mulungu weniweniyo. N’chifukwa chake, pa Yoh 1:1 mu Baibulo la Dziko Latsopano Lomasulira Malemba Achigiriki Achikhristu, tinalemba “mulungu” wa “m” wamng’ono m’mawu akuti “komanso Mawuyo anali mulungu,” pofuna kum’siyanitsa ndi Mulungu weniweniyo amene nthawi zonse timamulemba ndi “M” wamkulu.

a Lomasuliridwa kuchokera ku Chifalansa.

b Lomasuliridwa kuchokera ku Chifalansa.

c Lomasuliridwa kuchokera ku Chijeremani.

d Lomasuliridwa kuchokera ku Chijeremani.

e Lomasuliridwa kuchokera ku Chijeremani.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena