Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g89 6/8 tsamba 3
  • Kuyendayenda mu Imfa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyendayenda mu Imfa
  • Galamukani!—1989
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mphamvu ya Munthu Ingaletse Iwo?
    Galamukani!—1989
  • Lipoti la Mayiko Komanso Madera
    Lipoti la Chaka Chautumiki cha 2019 la Mboni za Yehova Padziko Lonse.
  • Zida Zazing’ono Koma Mavuto Aakulu
    Galamukani!—2001
  • Kodi Ndani Amene Angabweretse Mtendere Wokhalitsa?
    Galamukani!—1996
Onani Zambiri
Galamukani!—1989
g89 6/8 tsamba 3

Kuyendayenda mu Imfa

Pamene kuli kwakuti dziko likuwononga chifupifupi madola triliyoni imodzi pa chaka kaamba ka zida zankhondo:

Anthu 800,000,000 akukhala mu umphaŵi wotheratu

770,000,000 alibe chakudya chokwanira kaamba ka moyo wogwira ntchito mokangalika

100,000,000 alibe pogona

1,300,000,000 alibe madzi akumwa achisungiko

Ana 14,000,000 amafa chaka chirichonse chifukwa cha ziyambukiro za njala

IWO atchedwa Amalonda a Imfa, Okumba Manda a Kutsungula, Kansa Yotupa pa Thupi la Chitaganya. Ndani? Amalonda a zida zankhondo a dziko. Chifukwa ninji?

Mu nthaŵi zakale, iwo anasunga magulu ankhondo okonzekeretsedwa ndi malupanga, mikondo, nkhwangwa, ndi mivi kaamba ka kupha kwa munthu ndi munthu pa mabwalo ankhondo. M’zana lino, iwo anapanga ndi kugawira mfuti, mabomba, akasinja, zombo zankhondo, ndege, gas ya ululu, ndi zipolopolo zophera makumi a mamiliyoni a anthu mu nkhondo zadziko ziŵiri pamene panthaŵi imodzimodziyo akuwononga mabiliyoni a madola a magwero a chuma, onga ngati mizinda, nyumba, ndi katundu wina. Iwo anapangitsa nkhondo zoposa 120 zomenyedwa chiyambire mapeto a Nkhondo ya Dziko ya II.

Iwo akupitirizabe kupangitsa nkhondo zokhetsa mwazi mu mbali zosiyanasiyana za dziko. Iwo amaphunzitsa magulu ankhondo a Maiko Otukuka Kumene kaamba ka kugwiritsira ntchito kokhutiritsa kwa zida zawo. Iwo akonzekeretsa mphamvu zankhondo za dziko ndi mulu wa zida za nyukliya zokhoza kuphulitsa banja la anthu nthaŵi zingapo mobwerezabwereza ndi kusintha dziko lapansi kukhala pulaneti losakhalidwamo. Iwo akuwoneka kukhala osasamala kotheratu. Liwu lawo la kunyada lingakhale lakuti: “Imfa yanu—phindu lathu.”

Palibe malonda amene ayambukira banja la anthu mwakuya chotero monga malonda a zida zankhondo. Maumboni ali owonekera bwino. Nkhani yotsatira idzavumbula nsonga zina zovutitsa maganizo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena