Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g96 4/8 tsamba 32
  • Chiŵiya Chofunika kwambiri cha Maphunziro

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chiŵiya Chofunika kwambiri cha Maphunziro
  • Galamukani!—1996
Galamukani!—1996
g96 4/8 tsamba 32

Chiŵiya Chofunika kwambiri cha Maphunziro

Phungu wa nyumba ya malamulo wina ku dziko la Sri Lanka analembera “Mkonzi wa ‘Galamukani!’” Kalata yake yajambulidwa pansipa:

“Bwana Wokondedwa,

“Ndiyenera kunena kuti ngakhale kuti magazini a Galamukani! amene mumafalitsa ndi aang’ono, iwo ngwofunikadi ndipo amakhala apanthaŵi yake. Nkhani iliyonse imathandizira wachichepere wa m’tsiku lino kusiyanitsa bwinobwino chabwino ndi choipa.

“Ndaŵerenga nkhani zonse. Zimene ndaona nzakuti mphunzitsi wapasukulu aliyense, wophunzira, ndi kholo ayenera kuŵerenga magazini ameneŵa mosakayikira.

“Ndikuyamikira kwambiri ntchito yabwino imene mukuchita. Ndikukufunirani chipambano pa zoyesayesa zanu.”

Pafupifupi magazini mamiliyoni 16 a kope lililonse la Galamukani! amasindikizidwa, m’zinenero 78. Magaziniwa amadziŵika dziko lonse lapansi monga chiŵiya chofunika kwambiri cha maphunziro. Inunso mudzapindula mwa kuwaŵerenga. Ngati mungafune kope kapena ngati mungafune kukhala ndi phunziro la Baibulo lapanyumba laulere, chonde lemberani ku Watch Tower, Box 33459, Lusaka 10101, kapena ku keyala yoyenera yondandalitsidwa patsamba 5.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena