Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 10/12 tsamba 5
  • Muzikhala ndi Okuthandizani

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzikhala ndi Okuthandizani
  • Galamukani!—2012
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Ndingatani Kuti Ndizigwirizana Ndi Aphunzitsi Anga?
    Zimene Achinyamata Amafunsa
  • Kodi Ndingatani Kuti Ndizigwirizana Ndi Aphunzitsi Anga?
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Loyamba
  • N’Chifukwa Chiyani Timafunikira Aphunzitsi?
    Galamukani!—2002
  • Mfungulo Zopezera Maphunziro Abwino
    Galamukani!—1996
Onani Zambiri
Galamukani!—2012
g 10/12 tsamba 5

Muzikhala ndi Okuthandizani

Kukhala ndi anthu amene angamakulangizeni komanso kukuthandizani n’kofunika pamene muli pa sukulu komanso mukadzamaliza sukulu.

KODI ndani amene angakuthandizeni kuti zinthu zizikuyenderani bwino ku sukulu?

Anthu am’banja mwanu.

Mtsikana wina wazaka 18, wa ku Brazil, dzina lake Bruna, ananena kuti: “Homuweki ikakhala kuti yandivuta, bambo anga ankandifotokozera bwino kenako n’kundifunsa mafunso. Koma sankandiuzira mayankho chifukwa ankafuna kuti ndipeze ndekha.”a

Mfundo yothandiza: Funsani makolo anu kuti anene mmene ankakhozera phunziro limene limakuvutanilo. Ngati ankakhoza bwino, ndiye kuti angakuthandizeni.

Aphunzitsi.

Aphunzitsi ambiri amasangalala akaona kuti mwana wasukulu akufunitsitsa kuti azikhoza bwino ndipo amayesetsa kuti amuthandize.

Mfundo yothandiza: Mungachite bwino kuwauza aphunzitsi anu kuti: “Ndimafuna nditamakhoza bwino phunziroli koma limandivuta. Kodi mungandithandize bwanji?”

Anthu ena okuthandizani.

Mwina munthu wina amene mumamudalira akhoza kukuthandizani. Zimenezi zingakuthandizeni m’njira ziwiri izi: Choyamba, mungapeze thandizo limene mukufuna ndipo chachiwiri, mungaphunzire kudalira anthu ena, zomwenso zingadzakuthandizeni mukadzakula. Dziwani kuti munthu aliyense zimamuyendera bwino ngati anthu ena amuthandiza.​—Miyambo 15:22.

Mfundo yothandiza: Afunseni makolo anu kuti akuuzeni anthu ena amene iwo akuganiza kuti akhoza kukuthandizani.

Mfundo yofunika kuikumbukira: Palibe cholakwika ndi kupempha ena kuti akuthandizeni.

Yambani kutsatira malangizo amenewa. Lembani mayina a anthu awiri kapena atatu amene ndi zitsanzo zabwino ndipo mumafuna mutatengera chitsanzo chawo. Mwina mmodzi wa anthu amenewa akhoza kukuthandizani pa nkhani ya sukulu.

a Ngati muli ndi m’bale wanu wamkulu akhozanso kukuthandizani.

“Mphunzitsi amene ankandisangalatsa”

“Kale ndili pa sukulu, tinali ndi aphunzitsi enaake ovuta koma ana ankawalemekeza. Iwo ankakonda ntchito yawo kwambiri moti akamaphunzitsa ankayenda uku ndi uku m’kalasimo, uku akulankhula ndi manja. Iwo ankayesetsa kuti mwana aliyense azifotokoza maganizo ake. Nthawi zambiri ankakonda kutiuza kuti tizimasuka kuwafunsa mafunso. Iwo ankanena kuti kufunsa mafunso kungawathandize kudziwa zimene ifeyo sitikuzimvetsa komanso kuti akhale mphunzitsi wabwino. Ankasonyeza chidwi kwa mwana aliyense. Mwachitsanzo ukakhala kuti sunamvetse mfundo inayake, ankakufotokozera moleza mtima mpaka umvetse. Iwo anatiphunzitsa kwa chaka chimodzi phunziro la Accounts moti ana ambiri anasankha kuti adzagwira ntchito imeneyi.”​—Anatero Alana, wa ku Australia.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena