Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 9/14 tsamba 16
  • Chimene Chimachititsa Kuti Dzombe Lisamawombane Pouluka

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chimene Chimachititsa Kuti Dzombe Lisamawombane Pouluka
  • Galamukani!—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Tsiku la Yehova Layandikira
    Nsanja ya Olonda—1998
  • Zamkatimu
    Galamukani!—2014
  • Kumbukirani Tsiku la Yehova
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Tsoka Loyamba Linali Dzombe
    Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
Onani Zambiri
Galamukani!—2014
g 9/14 tsamba 16
Dzombe lochuluka likuuluka

KODI ZINANGOCHITIKA ZOKHA?

Chimene Chimachititsa Kuti Dzombe Lisamawombane Pouluka

DZOMBE limauluka m’magulu ndipo nthawi zina limauluka lokwana 80 miliyoni pa gulu limodzi. Komatu dzombeli siliwombana. Kodi chinsinsi chake chagona pati?

Taganizirani izi: Pakati pa maso a dzombeli pamakhala maselo amene amatumiza uthenga ku ubongo. Dzombe likatsala pang’ono kuwombana ndi linzake, maselowa amatumiza uthenga kumapiko ndi miyendo ndipo izi zimapangitsa kuti dzombelo lichite zinthu mwachangu kuti lisawombane ndi linalo. Uthengawu umayenda mofulumira kwambiri moti inuyo mukaphethira kamodzi, maselowa amakhala atatumiza mauthenga ka 5.

Potengera maso komanso maselo a dzombeli, asayansi apanga loboti imene imatha kuzindikira chinthu chimene chili pafupi pake n’kuchizemba kuti zisawombane. Asayansiwa apanga lobotili pogwiritsa ntchito pulogalamu inayake yapakompyuta. Pofuna kuchepetsa kuwombana kwa magalimoto, akatswiri a sayansi akugwiritsa ntchito luso limeneli n’kumapanga magalimoto okhala ndi loboti yothandiza kuti galimotoyo izizindikira mwachangu kuti yatsala pang’ono kuwombana ndi inzake. Pulofesa wina, wa pa yunivesite ya Lincoln ku United Kingdom, dzina lake Shigang Yue ananena kuti: “Pali zambiri zimene tingaphunzire kuchokera ku tizilombo ting’onoting’ono monga dzombe.”

Kodi inuyo mukuganiza bwanji? Kodi zinangochitika zokha kuti dzombe likhale ndi maselo omwe amatumiza uthenga mofulumira chonchi, kapena pali winawake amene anawapanga?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena