Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 15
  • Mkazi wa Loti Anacheuka

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mkazi wa Loti Anacheuka
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Kumbukirani Mkazi wa Loti
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Konzekerani Kaamba ka Chipulumutso Kuloŵa M’dziko Latsopano
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Mulungu Anachita Pangano ndi Abulahamu
    Kodi Baibulo Lili Ndi Uthenga Wotani?
  • Tizithandiza Anthu Amene Ali ndi Nkhawa
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 15

NKHANI 15

Mkazi wa Loti Anacheuka

LOTI ndi banja lake anakhala ndi Abrahamu m’Kanani. Tsiku lina Abrahamu anati kwa Loti: ‘Palibe malo okwanira zifuyo zathu zonse. Tilekanetu. Ukamka uku, ine ndidzamka kwinako.’

Loti anayang’ana dziko’lo. Anaona chigawo chabwino kwambiri cha madzi ambiri ndi msipu wochuluka kaamba ka zifuyo zake. Ichi chinali Chigawo cha Yordano. Chotero Loti anasamutsira banja lake ndi zifuyo kumene’ko. Potsirizira pake anamanga nyumba yao mu mzinda wa Sodumu.

Anthu a Sodomu anali oipa kwambiri. Izi zinabvutitsa Loti chifukwa anali wabwino. Mulungu’nso anabvutika maganizo. Kenako, Mulungu anatumiza angelo awiri kukachenjeza Loti kuti akaononga Sodomu ndi Gomora chifukwa cha kuipa kwao.

Iwo anauza Loti kuti: ‘Fulumira! Tenga mkazi wako ndi ana ako akazi awiri nutuluke muno!’ Iwo anali ochedwa pang’ono, chotero angelo’wo anawagwira pa dzanja nawatulutsa mu mzinda’wo. M’modzi wa angelo’wo anati: ‘Thawitsani miyoyo yanu! Musacheuke. Thamangirani ku mapiri, kuti musaphedwe!’

Loti ndi ana ake anamvera nathawa m’Sodomu. Iwo sanaime, ndipo sanacheuke. Koma mkazi wa Loti sanamvere. Atayenda mtunda pang’ono kuchoka m’Sodomu, anaima nacheuka. Pompo anakhala chulu cha mchere. Kodi mukumuona m’chithunzi’mo?

Tikuphunziramo phunziro labwino. Zimasonyeza kuti Mulungu amapulumutsa awo amene amamvera, koma awo amene samamumvera adzataya miyoyo yao.

Genesis 13:5-13; 18:20-33; 19:1-29; Luka 17:28-32; 2 Petro 2:6-8.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena