Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gf phunziro 6 tsamba 10-11
  • Paradaiso Ali Pafupi

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Paradaiso Ali Pafupi
  • Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Nkhani Yofanana
  • Moyo Wabwino Kwambiri—Posachedwapa!
    Nsanja ya Olonda—1995
  • Kodi Paradaiso Adzabwera Liti?
    Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha
  • Kodi Tilidi ‘M’masiku Otsiriza’?
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
  • “Mapeto a Dziko” Ayandikira!
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
Onani Zambiri
Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
gf phunziro 6 tsamba 10-11

PHUNZIRO 6

Paradaiso Ali Pafupi!

Zoipa zimene zikuchitika padziko lapansi zimasonyeza kuti Paradaiso ali pafupi. Baibulo linanena kuti tidzaona nthaŵi zoipitsitsa pamene Paradaiso wayandikira. Nthaŵi zake ndi zinozi! Nazi zina mwa zimene Baibulo linati zidzachitika:

Ndege za Nkhondo

Nkhondo zazikulu. “Mtundu umodzi wa anthu udzaukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu ndi ufumu wina.” (Mateyu 24:7) Ulosi umenewu wakwaniritsidwa. Kuchokera m’chaka cha 1914, pachitika nkhondo zapadziko lonse ziŵiri ndi zing’onozing’ono zambiri. Anthu mamiliyoni aphedwa m’nkhondo zimenezo.

Matenda ofalikira. Kudzakhala “miliri m’malo akutiakuti.” (Luka 21:11) Kodi zimenezi zachitikadi? Inde. Kansa, matenda a mtima, chifuŵa cha TB, malungo, AIDS, ndi matenda ena apha anthu mamiliyoni ambiri.

Odwala, anthu akuvutika

Kusoŵa chakudya. Kuzungulira dziko lonse lapansi pali anthu amene sadya mokwanira. Mamiliyoni a anthu amafa ndi njala chaka chilichonse. Chimenechi ndi chizindikiro china chakuti Paradaiso wayandikira. Baibulo limati: “Padzakhala njala.”—Marko 13:8.

Zivomezi. “Kudzakhala . . . zivomezi m’malo akutiakuti.” (Mateyu 24:7) Izinso zachitika m’nthaŵi yathu. Anthu oposa miliyoni imodzi afa m’zivomezi chiyambire 1914.

Munthu ali ndi mfuti ndipo wagwira mayi wina

Anthu oipa. Anthu adzakhala “okonda ndalama” ndi “odzikonda okha.” Adzakhala “okonda zokondweretsa osati okonda Mulungu.” Ana akakhala “osamvera akuwabala.” (2 Timoteo 3:1-5) Kodi simukuvomereza kuti anthu oterowo alipo ambiri lero? Iwo alibiretu ulemu kwa Mulungu, ndipo amavutitsa aja omwe amayesa kuphunzira za Mulungu.

Upandu. Padzakhalanso “kuchuluka kwa kusayeruzika.” (Mateyu 24:12) Mwachionekere inunso mukuvomereza kuti upandu tsopano wafika poipa kusiyana ndi zaka za m’mbuyomu. Anthu kulikonse amakhala pangozi ya kuberedwa, kunamizidwa, kapena kuvulazidwa.

Zinthu zonsezi zimasonyeza kuti Ufumu wa Mulungu wayandikira. Baibulo limati: “Pakuona zinthu izi zilikuchitika, zindikirani kuti Ufumu wa Mulungu uli pafupi.” (Luka 21:31) Kodi Ufumu wa Mulungu ndi chiyani? Ndi boma la Mulungu lakumwamba limene lidzabweretsa Paradaiso padziko lapansili. Ufumu wa Mulungu udzaloŵa m’malo mwa maboma onse a anthu.—Danieli 2:44.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena