Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gf phunziro 15 tsamba 24-25
  • Mabwenzi a Mulungu Amachita Zabwino

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mabwenzi a Mulungu Amachita Zabwino
  • Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Nkhani Yofanana
  • Zimene Mungachite Kuti Banja Lanu Lizisangalala
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Makiyi Aŵiri a Ukwati Wokhalitsa
    Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
  • Moyo wa Banja Umene Umakondweretsa Mulungu
    Kodi Mulungu Amafunanji kwa Ife?
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kulemekeza Ulamuliro?
    Kodi Mungatani Kuti Mulungu Azikukondani?
Onani Zambiri
Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
gf phunziro 15 tsamba 24-25

PHUNZIRO 15

Mabwenzi a Mulungu Amachita Zabwino

Pamene muli ndi mnzanu amene mumam’sirira ndi kum’lemekeza, mumayesa kum’tsanzira. Baibulo limanena kuti “Yehova ndiye wabwino ndi wolunjika mtima.” (Salmo 25:8) Kuti tikhale mabwenzi a Mulungu, tiyenera tikhale abwino ndi owongoka mtima. Baibulo limati: “Khalani akutsanza a Mulungu, monga ana okondedwa; ndipo yendani m’chikondi.” (Aefeso 5:1, 2) Nazi njira zina zochitira zimenezi:

Azibambo awiri akuthandizana kumanga nyumba

Khalani wothandiza ena. “Tichitire onse chokoma.”—Agalatiya 6:10.

Gwirani ntchito zolimba. “Wakubayo asabenso; koma makamaka agwiritse ntchito, nagwire ntchito yokoma ndi manja ake.”—Aefeso 4:28.

Khalani waukhondo m’thupi ndi m’makhalidwe. “Tidzikonzere tokha kuleka chodetsa chonse cha thupi ndi cha mzimu, ndi kutsiriza chiyero m’kuopa Mulungu.”—2 Akorinto 7:1.

Banja likukonzekera kudya chakudya

Sonyezani apabanja panu chikondi ndi ulemu. “Yense payekha, . . . akonde mkazi wake wa iye yekha, monga adzikonda yekha; ndipo mkaziyo akumbukire kuti aziopa [“azilemekeza kwambiri”, NW] mwamuna. Ananu, mverani akukubalani.”—Aefeso 5:33–6:1.

Sonyezani chikondi kwa ena. “Tikondane wina ndi mnzake; chifukwa kuti chikondi chichokera kwa Mulungu.”—1 Yohane 4:7.

Mverani malamulo a dziko. “Anthu onse amvere maulamuliro aakulu [boma] . . . Perekani kwa anthu onse mangawa awo; msonkho kwa eni ake a msonkho.”—Aroma 13:1, 7.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena