Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yp1 tsamba 149
  • Chitsanzo Chabwino—Mose

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chitsanzo Chabwino—Mose
  • Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Loyamba
  • Nkhani Yofanana
  • Tsanzirani Chikhulupiriro cha Mose
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Mmene Moyo wa Mose Umakukhudzirani
    Galamukani!—2004
  • Mose Anali Munthu Wachikhulupiriro Cholimba
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Phunzirani Njira za Yehova
    Nsanja ya Olonda—2005
Onani Zambiri
Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Loyamba
yp1 tsamba 149

Chitsanzo Chabwino​—Mose

Mose anali ndi mwayi wambiri. Anakulira m’banja lachifumu la Farao ndipo anaphunzira nzeru zonse za Aiguputo. (Machitidwe 7:22) Kodi anagwiritsa ntchito bwanji zomwe anaphunzirazo? Mose akanatha kukhala wotchuka, wolemera komanso akanatha kukhala ndi udindo waukulu m’boma. Komabe, iye sanakopeke ndi zimene anzake ankachita kapena kufuna kutchuka. M’malomwake anasankha ntchito imene anthu ambiri sankayembekezera. Iye “anasankha kuzunzidwa pamodzi ndi anthu a Mulungu.” (Aheberi 11:25) Koma kodi kuchita zimenezi inali nzeru? Inde, chifukwa kusankha kwake kutumikira Mulungu ndiponso kuthandiza anthu, kunamuthandiza kuti azikhala wosangalala.

Ngati muli ndi mwayi wophunzira kwambiri, kodi mudzachita chiyani pambuyo pomaliza sukulu? Mukhoza kusankha ntchito yabwino komanso kukhala ndi udindo waukulu. Komanso mofanana ndi Mose, muli ndi mwayi wogwiritsa ntchito moyo wanu pa zinthu zaphindu kwambiri. Mukhoza kugwiritsa ntchito maphunziro anu komanso mphamvu zimene muli nazo potumikira Mulungu ndiponso anthu ena. (Mateyu 22:35-40) Palibe ntchito ina yabwino komanso yaphindu kwambiri kuposa imeneyi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena