Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w88 4/15 tsamba 31
  • Kodi Mumakumbukira?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mumakumbukira?
  • Nsanja ya Olonda—1988
  • Nkhani Yofanana
  • Nthaŵi ya Kufika kwa Mesiya Ivumbulidwa
    Samalani Ulosi wa Danieli!
  • Mmene Ulosi wa Danieli Unasonyezera Nthawi Imene Mesiya Adzafike
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
  • Kulani M’chikondi
    Nsanja ya Olonda—2001
  • Kodi Ndimapemphero Ayani Omwe Amayankhidwa?
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—1988
w88 4/15 tsamba 31

Kodi Mumakumbukira?

Kodi mwasangalala kuŵerenga makope aposachedwapa a Nsanja ya Olonda? Chabwino, onani ngati mungakhoze kuyankha mafunso otsatirawa:

◻ Kodi nchiyani chimene chiri mutu wa kulengeza kwamakono kwa m’Baibulo?

Mutu wa uthenga wa alengezi owona lerolino uli mbiri yabwino ya Ufumu wa Mulungu m’manja mwa wolamulira wake woikidwa, Yesu Kristu. Iwo umaphatikizapo chowonadi chonse chimene Yesu analankhula ndi chimene ophunzira ake anachilemba. (Mateyu 24:14; 28:19, 20)​—1/1, tsamba 4.

◻ Nchifukwa ninji chiri choyenerera kupitirizabe kulalikira mbiri yabwino m’magawo mmene muli zotulukapo zochepa kapena kulibiretu?

Yehova, kupyolera mwa Kristu Yesu, walamulira kuti ‘mbiri yabwino imeneyi ilalikidwe m’dziko lonse lokhalidwa ndi anthu.’ (Mateyu 24:14, NW) Pamene anthu akana kumvetsera, ichi chimatipatsa ife mwaŵi wosonyeza kuzama kwa chikondi chathu ndi kudzipereka kwa Yehova mwa kuumirira kuchita chimene chiri chabwino. Ndiponso, chikondi chathu chimatisonkhezera ife kuchenjeza anansi athu ponena za chimene mtsogolo mwasunga kaamba ka mtundu wa anthu. (1 Yohane 5:3; 2 Timoteo 4:2)​—1/1, tsamba 26.

◻ Ndi mapindu otani amene utumiki wa nthaŵi zonse umabweretsa kwa olalikira Ufumu ambiri?

Umawathandiza iwo kukulitsa mokwanira koposa chipatso cha mzimu, kusonyeza chikondi chochulukira cha anthu, kukhala okhutiritsa kwenikweni mu utumiki, ndi kukhulupirira Yehova ku mlingo wokulira. Chotero, iwo amasangalala ndi unansi wa thithithi ndi Yehova.​—1/15, tsamba 26.

◻ Ndi ku chitsogozo chiti ndi chifuno cha Mulungu kumene olemba Baibulo onse analoza mosasamala kanthu za kusiyana kwawo m’kaperekedwe?

Iwo onse anasonyeza chimene Yehova Mulungu adzachita kupangitsa mtundu wa anthu kukhala wachimwemwe ndiponso chimene munthu aliyense payekha ayenera kuchita ndi cholinga chofuna kulandira chivomerezo cha Mulungu.​—2/1, tsamba 7.

◻ Ndi ziti zimene ziri mphatso zina ndi mapindu a kukhala owona mtima?

Mkhalidwe wa kukhulupirira ndi kudalira umakulitsidwa, kutsogolera ku mkhalidwe waumoyo ndi maunansi. Kuwona mtima kumathandiziranso kukhala ndi chikumbumtima choyera, ndipo kumapereka mtendere wa maganizo, kotero kuti wina angayang’anizane ndi ena popanda mantha akuchititsidwa manyazi. (Ahebri 9:14; 1 Timoteo 1:19)​—2/15, tsamba 7.

◻ Ndi mapemphero andani amene Mulungu wamphamvuyonse amamva ndi kuyankha?

Yehova amamva mapemphero operekedwa kwa iye kupyolera mu ngalande yoyenera, Yesu Kristu; mu mkhalidwe wabwino; ndipo ndi cholinga chabwino cha maganizo ndi mtima. Mulungu amayankha mapemphero oterowo mogwirizana ndi chifuno chake chaumulungu ndipo pa nthaŵi yake yosankhidwa.​—3/15, tsamba 7.

◻ Ndi chochitika chofunika chotani chimene chinawoneka mu chaka cha 20 cha kulamulira kwa Mfumu Aretasasta (455 B.C.E.)?

Chilolezo chinaperekedwa kwa Nehemiya kubwerera ndi kukamanganso Yerusalemu ndi malinga ake. Lamulo limeneli linali chiyambi cha “milungu makumi asanu ndi aŵiri” a zaka za ulosi wa Danieli, kulozera kutsogolo ku kuwoneka kwa Yesu monga “Mesiya Mtsogoleri” pa nthaŵi yake m’chaka cha 29 C.E. (Danieli 9:24, 25; Nehemiya 1:1; 2:1-9)​—3/15, masamba 28, 29.

◻ Ndimotani mmene mavuto abanja amasamaliridwira bwino koposa?

M’chikondi, popeza Baibulo limapatsa uphungu kuti, “Zanu zonse zichitike m’chikondi.” Ndiponso, “Chikondano chikwiriritsa unyinji wa machimo.” (1 Akorinto 16:14; 1 Petro 4:8) Ichi chiyenera kukhala chikondi chozama chomwe chiri chofunitsitsa kunyalanyaza kupanda ungwiro kwa ziwalo zina za banja zomwe mwa njira ina yake zingakwiitse kapena kukalipitsa ena.​—4/1, masamba 6, 7.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena