Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w93 4/1 tsamba 32
  • Chochitika Chofunika Koposa m’Mbiri

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chochitika Chofunika Koposa m’Mbiri
  • Nsanja ya Olonda—1993
Nsanja ya Olonda—1993
w93 4/1 tsamba 32

Chochitika Chofunika Koposa m’Mbiri

Kodi nchifukwa ninji chili chotero? Chochitikacho chinali imfa ya Yesu Kristu.

Chinachititsa kulemekezedwa kwa uchifumu wa Mulungu ndi kutsimikizira kuti munthu akhoza kusunga umphumphu wokwanira kwa Mulungu. Chinapereka kwa anthu chiyembekezo chakupeza moyo wosatha m’mikhalidwe yaparadaiso. Yesu mwiniyo anayambitsa chikumbutso cha imfa yake usiku asanafe.

Chinali dzoma losacholoŵana. Padzomalo, Yesu anauza ophunzira ake kuti: “Chitani ichi chikumbukiro changa.” (Luka 22:19, 20) Kodi mudzakumbukira? Mboni za Yehova zikukuitanani kugwirizana nazo kuchita phwando limeneli lofunika koposa m’mbiri. Chaka chino lidzakhalako pa Lachiŵiri, April 6, dzuŵa litaloŵa.

Chonde funsani pa Nyumba Yaufumu yapafupi nanu ponena za nthaŵi yeniyeni ndi malo. Palibe zopereka zimene zidzatengedwa, ndipo alendo akuitanidwa kudzamvetsera nkhani yophunzitsa ndi kuwona zochitika zosavuta.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena