Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w01 6/15 tsamba 32
  • “Kulasa kwa Bwenzi”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Kulasa kwa Bwenzi”
  • Nsanja ya Olonda—2001
Nsanja ya Olonda—2001
w01 6/15 tsamba 32

“Kulasa kwa Bwenzi”

MTUMWI Paulo anaona kuti kunali kofunika kudzudzula zolakwika pakati pa Akristu a m’zaka za zana loyamba a ku Galatiya. Koma pofuna kupewa kuwakwiyitsa, iye anafunsa kuti: “Kotero kodi ndasanduka mdani wanu, pakukunenerani zoona?”​—Agalatiya 4:16.

‘Ponena zoona,’ Paulo sanakhale mdani wawo. Iye anatero mogwirizana ndi mfundo yachikhalidwe ya m’Baibulo yakuti: “Kulasa kwa bwenzi kuli kokhulupirika.” (Miyambo 27:6) Anadziŵa kuti anthu olakwawo akhumudwa. Anadziŵanso kuti kupewa kulangiza wolakwa ndiko kukana kum’sonyeza chikondi cha Yehova Mulungu. (Ahebri 12:5-7) Choncho, pokhala bwenzi lokhulupirika la mpingowo ndi poufunira zabwino nthaŵi zonse, Paulo sanapeŵe kudzudzula kuti akonze zinthu.

Masiku ano, Mboni za Yehova zikugwira ntchito yawo ‘yophunzitsa anthu a mitundu yonse, . . . kuwaphunzitsa, asunge zinthu zonse zimene [Yesu Kristu] walamula.’ Pochita zimenezo, Akristu okhulupirika ameneŵa, sapeŵa kufotokoza choonadi cha m’Baibulo chomwe chimavumbula ndi kutsutsa ziphunzitso zolakwika ndi makhalidwe osayenera Akristu. (Mateyu 15:9; 23:9; 28:19, 20; 1 Akorinto 6:9, 10) Sachita zimenezi kuti anthu ena aziwada. Iwo akusonyeza chidwi chimene mabwenzi enieni amasonyeza.

Mouziridwa ndi Mulungu, wamasalmo analemba kuti: “Akandipanda munthu wolungama ndidzati n’chifundo: akandidzudzula, ndidzakuyesa mafuta a pamutu; mutu wanga usakane: pakuti pangakhale posautsidwa iwo ndidzawapempherera.”​—Salmo 141:5.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena