Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w06 4/1 tsamba 32
  • Kodi Mulungu Ali ndi Mphamvube?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mulungu Ali ndi Mphamvube?
  • Nsanja ya Olonda—2006
Nsanja ya Olonda—2006
w06 4/1 tsamba 32

Dzamvereni Nkhani Yakuti . . .

Kodi Mulungu Ali ndi Mphamvube?

TSIKU sililowa popanda kumva nkhani za zinthu monga masoka achilengedwe, matenda oopsa, akuluakulu ochita zakatangale, uchigawenga, nkhondo, kapena umbanda. Kaya nkhanizi zimakukhudzani inuyo kapena ayi, n’zosakayikitsa kuti mumadzifunsa kuti dzikoli likulowera kuti ndiponso kuti kodi zinthu zisintha?

Pofuna kuyankha mafunso amenewa, Mboni za Yehova m’mayiko opitirira 200 padziko lonse zidzakhala ndi nkhani ya anthu onse ya mutu wakuti “Kodi Mulungu Ali ndi Mphamvube pa Zochitika za Padziko Lapansi Pano?” Nkhaniyi idzalongosola zimene Mulungu amanena ndi kulonjeza m’Mawu ake osanama, Baibulo, pa mafunso ofunika otsatirawa:

Kodi Mulungu amaganizira zochitika za padziko lapansi pano?

Kodi anthu amawaona bwanji?

Kodi inuyo amakuganizirani pa moyo wanu?

M’madera ambiri nkhaniyi idzakambidwa Lamlungu, pa April 30, 2006, ku Nyumba ya Ufumu ya Mboni za Yehova. Mboni za kwanuko zingasangalale kukuuzani nthawi ndi malo amene akakambire nkhaniyi.

Mukuitanidwa ndi manja awiri kukamvetsera nkhani yolimbikitsa ya m’Baibuloyi yomwe n’njaulere ndipo idzayankha mokhutiritsa funso lakuti: Kodi Mulungu Ali ndi Mphamvube pa Zochitika za Padziko Lapansi Pano?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena