Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w09 4/1 tsamba 5
  • Kodi Kubadwa Mwatsopano N’kofunika Motani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Kubadwa Mwatsopano N’kofunika Motani?
  • Nsanja ya Olonda—2009
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Kubadwanso Ndiyo Njira Yopezera Chipulumutso?
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Kodi Kubadwa Mwatsopano Ndi Nkhani Yoti Munthu Amachita Kusankha Yekha?
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Kodi Kubadwanso Kumatanthauza Chiyani?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Yesu Anaphunzitsa Nikodemo
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2009
w09 4/1 tsamba 5

Kodi Kubadwa Mwatsopano N’kofunika Motani?

POKAMBIRANA ndi Nikodemo, Yesu anatsindika mfundo yakuti kubadwa mwatsopano, kapena kuti kubadwanso, n’kofunika kwambiri. Kodi iye anasonyeza motani zimenezi?

Taonani mmene Yesu anasonyezera kufunika kobadwa mwatsopano pokambirana ndi Nikodemo. Iye anati: “Munthu sangathe kuona ufumu wa Mulungu atapanda kubadwanso.” (Yohane 3:3) Mawu akuti “sangathe” ndiponso “atapanda” akusonyeza kufunika kobadwa mwatsopano. Mwachitsanzo, munthu atanena kuti, “Dzuwa litapanda kutuluka, kunja sikungache,” akutanthauza kuti dzuwa n’lofunika kwambiri kuti kunja kuche. Mofanana ndi zimenezi, Yesu ananena kuti kubadwanso n’kofunika kwambiri kuti munthu aone Ufumu wa Mulungu.

Pomalizira, Yesu ananena mawu otsatirawa pofuna kutsindika mfundoyi. Iye anati: “Anthu inu muyenera kubadwanso.” (Yohane 3:7) Choncho, malinga ndi zimene Yesu ananenazi, kuti munthu ‘akalowe mu Ufumu wa Mulungu,’ ayenera kubadwanso.​—Yohane 3:5.

Yesu anaona kuti kubadwa mwatsopano n’kofunika kwambiri. Choncho, Akhristu ayenera kuonetsetsa kuti nkhani imeneyi akuyimvetsa bwino. Mwachitsanzo, kodi mukuganiza kuti Mkhristu angasankhe yekha kuti abadwenso?

[Mawu Otsindika patsamba 5]

“Dzuwa litapanda kutuluka, kunja sikungache”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena