Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp19 No. 1 tsamba 15
  • Kodi Kudziwa Mulungu Kungakuthandizeni Bwanji?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Kudziwa Mulungu Kungakuthandizeni Bwanji?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2019
  • Nkhani Yofanana
  • Musasiyane ndi Yehova
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Kodi N’chiyani Chingakuthandizeni Kudziwa Bwino Mulungu?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Mulungu Ndiye Bwenzi Labwino Koposa, Limene Mungakhale Nalo
    Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Palibe Chinthu Chabwino Kwambiri Kuposa Kukhala pa Ubwenzi Ndi Mulungu
    Nsanja ya Olonda—2014
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2019
wp19 No. 1 tsamba 15
Anthu akusangalala m’Paradaiso

Kodi Kudziwa Mulungu Kungakuthandizeni Bwanji?

Mfundo zimene taphunzira munkhani zapitazi zatithandiza kupeza yankho la funso lakuti, Kodi Mulungu ndi ndani? Kuchokera m’Baibulo taphunzira kuti dzina lake ndi Yehova ndipo khalidwe lake lalikulu ndi chikondi. Taonanso zimene anachita kale komanso zimene adzachite m’tsogolo kuti athandize anthu. Koma padakali zambiri zimene mungaphunzire zokhudza Mulungu. Komabe mwina mungadzifunse kuti, Kodi kuphunzira zimenezi kundithandiza bwanji?

Yehova amatilonjeza kuti ‘tikam’funafuna, adzalola kuti tim’peze.’ (1 Mbiri 28:9) Taganizirani madalitso apadera amene tingapeze tikamufunafuna ndiponso kumudziwa Mulungu, omwe ndikukhala pa “ubwenzi wolimba ndi Yehova.” (Salimo 25:14) Kodi ubwenzi umenewu ungakuthandizeni bwanji?

Kukhala wosangalala. Baibulo limati Yehova ndi “Mulungu wachimwemwe.” (1 Timoteyo 1:11) Kukhala naye pa ubwenzi ndiponso kumutsanzira kungakuthandizeni kuti muzikhala wosangalala ndipo zimenezi zingachititse kuti mukhale ndi thanzi labwino. (Salimo 33:12) Komanso mungathe kupewa makhalidwe oipa, kukhala ndi makhalidwe abwino komanso kukhala bwino ndi ena. Kuchita zimenezi kungakuthandizeninso kuti muzikhala wosangalala. Mungayambe kukhala ndi maganizo ofanana ndi amene wolemba Masalimo wina anali nawo. Iye anati: “Kwa ine kuyandikira kwa Mulungu ndi chinthu chabwino.”​—Salimo 73:28.

Kusamaliridwa. Yehova analonjeza atumiki ake kuti: “Ndidzakupatsa malangizo ndi kukuyang’anira.” (Salimo 32:8) Zimenezi zikusonyeza kuti Yehova amasamalira mtumiki wake aliyense mogwirizana ndi zimene akufunikira. (Salimo 139:1, 2) Mukayesetsa kukhala pa ubwenzi wolimba ndi Yehova, mudzaona kuti nthawi zonse amakhala wokonzeka kukuthandizani.

Tsogolo labwino. Kuwonjezera pa kukuthandizani kukhala ndi moyo wosangalala panopa, Yehova Mulungu akukupatsaninso mwayi wokhala ndi tsogolo labwino. (Yesaya 48:17, 18) Baibulo limati: “Pakuti moyo wosatha adzaupeza akamaphunzira ndi kudziwa za inu, Mulungu yekhayo amene ali woona, ndi za Yesu Khristu, amene inu munamutuma.” (Yohane 17:3) Mu nthawi yovuta ino, chiyembekezo chimene Mulungu watipatsa chimakhala ngati nangula chifukwa chimatithandiza kuti tisagwedezeke.​—Aheberi 6:19.

Zimene takambiranazi ndi zifukwa zochepa chabe zotichititsa kufuna kuti timudziwe bwino Mulungu komanso tikhale naye pa ubwenzi. Kuti mudziwe zambiri, funsani wa Mboni za Yehova aliyense kapena pitani pa webusaiti yathu ya jw.org/ny.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena