Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 1/99 tsamba 7
  • Zilengezo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zilengezo
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
km 1/99 tsamba 7

Zilengezo

◼ Mabuku ogaŵira mu January: Lililonse la mabuku a masamba 192 limene mpingo ungakhale nalo. February: Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja. March: Chidziŵitso Chotsogolera ku Moyo Wosatha. Tidzayesetsa kuyambitsa maphunziro a Baibulo apanyumba. April: Makope a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani!. Khalani ndi bolosha la Mulungu Amafunanji kaamba ka anthu ochita chidwi, ndipo yesetsani kuyambitsa maphunziro a Baibulo a panyumba.

◼ Ofalitsa onse obatizidwa amene adzapezeka pa Msonkhano Wautumiki wa mlungu wa January 4 adzapatsidwa makadi a Chidziŵitso kwa Dokotala/Chommasula ku Mlandu ndi ma Identity Card a ana awo.

◼ Kuyambira mu February, nkhani yatsopano ya oyang’anira dera idzakhala yakuti “Kodi Mulungu ndi Weniweni Motani kwa Inu?”

◼ Mipingo ikonzekere kuchita Chikumbutso chaka chino pa Lachinayi, April 1, dzuŵa litaloŵa. Ngakhale kuti nkhani ingayambe mofulumira, kuyendetsa zizindikiro za Chikumbutso sikuyenera kuchitika mpaka dzuŵa litaloŵa. Fufuzani kwa anthu odziŵa zanyengo kwanuko kuti mutsimikizire nthaŵi pamene dzuŵa lidzaloŵa m’dera lanu. Ngakhale kuti mpingo uliwonse ungafune kuchita Chikumbutso pawokha, nthaŵi zina zimenezi sizingatheke. Kumene mipingo ingapo imagwiritsa ntchito Nyumba ya Ufumu imodzi, mwina mpingo umodzi kapena yoposerapo ingapeze malo ena oti agwiritse ntchito madzulo amenewo. Tikupereka malingaliro akuti, ngati kuli kotheka, pologalamu ina ikatha pazipita mphindi zosachepera 40 ina isanayambe kuti mukhale ndi nthaŵi yokwanira yolonjera alendo, kulimbikitsa amene angoyamba kumene kusangalatsidwa, ndi kuti nthaŵiyo mupindule nayo mokwanira. Muyeneranso kulingalira za vuto la magalimoto ndi malo oimikapo magalimotowo, kuphatikizapo kusiya ndi kunyamula anthu. Bungwe la akulu liyenera kusankha makonzedwe amene angakhale abwino kwambiri kaamba ka mpingo wawo.

◼ Nkhani yapoyera yapadera ya nyengo ya Chikumbutso cha 1999 idzakambidwa pa Lamlungu, April 18. Mutu wake udzakhala wakuti “Ubwenzi Weniweni ndi Mulungu ndi Mnansi.” Autilayini yake tidzatumiza. Mipingo imene mlungu umenewo idzakhala ikuchezeredwa ndi woyang’anira dera, msonkhano wadera, kapena tsiku la msonkhano wapadera idzakhala ndi nkhaniyi mlungu wotsatira. Palibe mpingo umene uyenera kukhala ndi nkhaniyi lisanafike tsiku la April 18, 1999.

◼ Zofalitsa Zomwe Zilipo:

The Time for True Submission (lokonzedwera Asilamu)—Chingelezi

Kalenda ya Mboni za Yehova ya 1999—Chicheŵa, Chingelezi

◼ Makaseti Atsopano Omwe Alipo:

Keep Your Eye Simple—Chingelezi

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena