Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/04 tsamba 3
  • Zilengezo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zilengezo
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 5/04 tsamba 3

Zilengezo

◼ Mabuku ogaŵira mu May: Gaŵirani magazini a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! Popanga maulendo obwereza kwa anthu achidwi, omwe ena mwa iwo angakhale amene anapezeka pa Chikumbutso kapena pa zochitika zina zauzimu koma sasonkhana ndi mpingo mokhazikika, yesetsani kugaŵira buku la Lambirani Mulungu. Tichite zotheka kuyambitsa phunziro la Baibulo lapanyumba, makamaka ngati ena anamaliza kale kuphunzira buku la Chidziŵitso ndi bulosha la Mulungu Amafunanji. June: Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso. Ngati anthu anena kuti alibe ana, gaŵirani bulosha la Mulungu Amafunanji. Pogwiritsa ntchito buloshali, yesetsani kuyambitsa maphunziro a Baibulo apanyumba. July ndi August: Mabulosha alionse amene mpingo uli nawo.

◼ Woyang’anira wotsogolera kapena wina amene iye wamusankha aŵerengere maakaunti a mpingo pa June 1 kapena patangodutsa masiku ochepa kuchoka pa detili. Mukatha kuŵerengerako, lengezani kumpingo mukamaliza kuŵerenga lipoti lotsatira la maakaunti.

◼ Zopereka za m’macheke zizilembedwa kuti ndalamazo apatse “Watch Tower.” Adiresi ya ofesi ya nthambi ndi Watch Tower Bible and Tract Society, P. O. Box 30749, Lilongwe 3. Macheke opita ku mpingo wanu azilembedwa kuti ndalamazo apatse mpingowo.

◼ Kuyambira ndi mabuku amene titumize mu July, mafomu a mpingo amene amatumizidwa chaka ndi chaka akhala akutumizidwa ku mipingo mafomuwo akakhalapo. Malangizo ofotokoza za kugaŵa mafomuŵa tidzawasonyeza pa mpambo wolongedzera mabuku. Ngati mipingo ingapo imagwiritsa ntchito Nyumba ya Ufumu imodzi, mtumiki wa mabuku ayenera kuonetsetsa kuti mpingo uliwonse walandira mafomu ake akangofika kumene.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena