Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 6/13 tsamba 8
  • Zochitika mu Utumiki Wakumunda

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zochitika mu Utumiki Wakumunda
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
km 6/13 tsamba 8

Zochitika mu Utumiki Wakumunda

Pa Mateyu 21:16 timawerenga kuti: “M’kamwa mwa ana ndi mwa ana oyamwa mwaikamo mawu otamanda.” Mogwirizana ndi zimenezi, tsiku lina kamtsikana kena ka zaka zitatu, dzina lake Estere, kankalalikira ndi mayi ake kunyumba ndi nyumba. Kenako anaima penapake kuti apume. Estere ataona amayi ena akudutsa, anaganiza zowalalikira. Anawapatsa kapepala kakuti, Sangalalani ndi Moyo Wabanja. Estere anangouza mayiwo kuti: “Kapepalaka kakunena za banja.” Mayiyo anasangalala kwambiri ndi kapepalako chifukwa anali ndi mavuto a m’banja. Izi zikusonyeza kuti ndi bwinodi kuphunzitsa ana athu kutamanda Yehova.—Miy. 22:6.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena