Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb22 March tsamba 5
  • Njira Zitatu Zimene Zingatithandize Kuti Tizidalira Yehova

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Njira Zitatu Zimene Zingatithandize Kuti Tizidalira Yehova
  • Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Nkhani Yofanana
  • Tili Ndi Mwayi Wopemphera kwa Mulungu
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Pemphero Lingakuthandizeni Kuti Mulungu Akhale Mnzanu
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Kodi Mumasankha Bwanji Zochita?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • Zosankha Zanu Zizilemekeza Mulungu
    Nsanja ya Olonda—2011
Onani Zambiri
Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
mwb22 March tsamba 5

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Njira Zitatu Zimene Zingatithandize Kuti Tizidalira Yehova

Davide anagonjetsa Goliyati chifukwa ankadalira Yehova. (1Sa 17:45) Yehova amafuna kusonyeza mphamvu zake kwa atumiki ake. (2Mb 16:9) Kodi tingasonyeze bwanji kuti timadalira nzeru za Yehova m’malo momadalira mphamvu kapena nzeru zathu? Onani njira zitatu zotsatirazi:

  • Tizipemphera nthawi zonse. Tisamangopemphera kuti Yehova atikhululukire tikalakwitsa chinachake koma kutinso atipatse mphamvu kuti tikwanitse kulimbana ndi mayesero. (Mt 6:12, 13) Tisamangopemphera kuti Yehova adalitse zomwe tasankha koma tizipempha kuti atitsogolere komanso atipatse nzeru tisanasankhe zochita.​—Yak 1:5

  • Tizikhala ndi ndandanda yowerengera komanso kuphunzira Baibulo. Tiziwerenga Baibulo tsiku lililonse. (Sl 1:2) Tiziganizira kwambiri zitsanzo za m’Baibulo komanso tizigwiritsa ntchito zimene tikuphunzirapo. (Yak 1:23-25) Tizikonzekera tikamapita mu utumiki m’malo momangodalira luso limene tili nalo. Tizikonzekera misonkhano kukadali nthawi n’cholinga choti tikapindule mokwanira

  • Tizichita zinthu mogwirizana ndi gulu la Yehova. Tizidziwa mfundo zatsopano zimene gulu likuyendera ndipo tizitsatira mwamsanga zinthu zikasintha. (Nu 9:17) Tizimvera akulu akamatipatsa malangizo komanso uphungu.​—Ahe 13:17

Apolisi akutengera m’bale m’ndende ndipo atolankhani ndi abale ena akuonerera.

ONERANI VIDIYO YAKUTI PALIBE CHIFUKWA CHOTI TIZIOPA KUZUNZIDWA, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

• Kodi abale ndi alongo ankaopa chiyani?

• Kodi n’chiyani chinawathandiza kuti athetse manthawa?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena