Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb24 March tsamba 2-3
  • March 4-10

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • March 4-10
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2024
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2024
mwb24 March tsamba 2-3

MARCH 4-10

MASALIMO 16-17

Nyimbo Na. 111 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. ‘Zinthu Zonse Zabwino Zimachokera kwa Yehova’

(10 min.)

Kukhala pa ubwenzi ndi anthu amene amatumikira Yehova kumatithandiza kukhala osangalala (Sl 16:2, 3; w18.12 26 ¶11)

Kudziwa kuti Yehova ndi mnzathu kumatithandiza kukhala osangalala kwambiri (Sl 16:5, 6; w14 2/15 29 ¶4)

Timamva kuti Yehova ali nafe chifukwa amatiteteza mwauzimu (Sl 16:8, 9; w08 2/15 3 ¶2-3)

Alongo awiri ahagana ku Nyumba ya Ufumu. Anthu ena akusangalala ndipo awazungulira.

Mofanana ndi Davide, timakhala ndi moyo wabwino kwambiri chifukwa chakuti nthawi zonse timachita zinthu zokhudza kulambira Yehova, yemwe amatipatsa zinthu zonse zabwino.

DZIFUNSENI KUTI, ‘Kodi panopa moyo wanga ukusiyana ndi mmene unalili ndisanaphunzire choonadi?’

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Sl 17:8​—Kodi mawu akuti “mwana wa diso lanu” amatanthauza chiyani? (it-2 714)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Sl 17:1-15 (th phunziro 5)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(1 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Mugawireni kapepala koitanira anthu ku Chikumbutso. (th phunziro 11)

5. Ulendo Woyamba

(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Mugawireni kapepala koitanira anthu ku Chikumbutso. Pambuyo poti munthuyo wasonyeza chidwi, yerekezerani kumuonetsa vidiyo yakuti Tizikumbukira Imfa ya Yesu, kenako kambiranani naye mfundo za muvidiyoyi. (th phunziro 9)

6. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Mugawireni kapepala koitanira anthu ku Chikumbutso. (th phunziro 2)

7. Kuphunzitsa Anthu

(5 min.) lff phunziro 14 mawu oyamba komanso mfundo 1-3 (th phunziro 6)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 20

8. Kodi Tingakonzekere Bwanji Chikumbutso?

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Mkate wopanda zofufumitsa komanso vinyo zili patebulo m’Nyumba ya Ufumu.

Pomvera lamulo la Yesu, Lamlungu pa 24 March, tidzakumbukira imfa yake, yomwe imaphatikizapo chikondi chapadera chimene Yehova ndi Yesuyo anatisonyeza. (Lu 22:19; Yoh 3:16; 15:13) Kodi tingakonzekere bwanji mwambo wapaderawu?

  • Mugwire ndi mtima wonse ntchito yoitanira anthu kuti adzamvetsere nkhani yapadera komanso adzapezeke pa Chikumbutso. Mukonze ndandanda ya anzanu amene mungawaitanire. Ngati ena mwa anzanuwo sakhala m’gawo la mpingo wanu, mungaone pa jw.org kuti mupeze nthawi ndi malo amene mwambowu ukachitikire m’dera limene amakhala

  • Mungawonjezere zochita mu utumiki m’mwezi wa March ndi April. Kodi mungachite upainiya wothandiza wa maola 15 kapena 30?

  • Pa 18 March, mudzayambe kuwerenga zinthu zikuluzikulu zomwe zinachitika pa wiki yomaliza ya moyo wa Yesu ali padzikoli. Mungasankhe kuchuluka kwa zomwe mungawerenge tsiku lililonse kuchokera pa “Ndandanda Yowerengera Baibulo pa Nyengo ya Chikumbutso cha 2024” yomwe ili patsamba 6-7

  • Pa tsiku la Chikumbutso, mudzaonere pulogalamu yapadera ya Kulambira kwa M’mawa pa jw.org

  • Pa Chikumbutso, mudzalandire mwansangala alendo komanso ofalitsa amene anasiya kusonkhana. Mudzakhale okonzeka kuyankha mafunso omwe anthuwa angakufunseni pambuyo pa mwambowu. Mudzakonze zoti mudzayendere anthu omwe adzabwere pa mwambowu kuti mukawathandize kuphunzira zambiri

  • Mwambo wa Chikumbutso usanachitike komanso ukadzatha, muzidzaganizira za dipo

Onerani VIDIYO yakuti Tizikumbukira Imfa ya Yesu. Kenako funsani funso lotsatirali:

Kodi tingagwiritse ntchito bwanji vidiyoyi pamene tikuitanira anthu ku Chikumbutso?

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) bt mutu 6 ¶18-24, bokosi patsamba 48

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 73 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena