Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 January tsamba 5-16
  • January 20-26

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • January 20-26
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 January tsamba 5-16

JANUARY 20-26

MASALIMO 138-139

Nyimbo Na. 93 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Musalole Kuti Mantha Akubwezeni M’mbuyo

(10 min.)

Timafuna kutamanda Yehova ndi mtima wathu wonse (Sl 138:1)

Ngati mumachita mantha kuyankha pamisonkhano, muzidalira Yehova kuti akuthandizeni (Sl 138:3)

Kuchita mantha kukhoza kukhala chizindikiro chabwino (Sl 138:6; w19.01 10 ¶10)

Mlongo wakweza dzanja kuti ayankhe pa misonkhano yampingo.

ZIMENE ZINGATITHANDIZE: Kupereka ndemanga zazifupi kungatithandize kuchepetsa mantha.—w23.04 21 ¶7.

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Sl 139:21, 22—Kodi Akhristu amayenera kukhululukira aliyense? (it-1 862 ¶4)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Sl 139:1-18 (th phunziro 2)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(3 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. (lmd phunziro 2 mfundo 3)

5. Kuphunzitsa Anthu

(4 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. M’pempheni kuti muziphunzira naye Baibulo ndipo musonyezeni mmene phunziroli limachitikira. (lmd phunziro 10 mfundo 3)

6. Nkhani

(5 min.) ijwyp 105—Mutu: Mungatani Kuti Musamachite Manyazi Kwambiri? (th phunziro 16)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 59

7. Mukhoza Kumasangalalabe ndi Utumiki Wanu Ngakhale Kuti Ndinu Wamanyazi

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Kodi ndinu wamanyazi? Kodi nthawi zambiri mumakonda kuti anthu asadziwe kuti mulipo? Kodi mumatuluka thukuta mukangoganizira kuti mukufunika kulankhula ndi anthu ena? Nthawi zina, kuchita manyazi kungatilepheretse kuchita zinthu zimene tingakonde kuchita. Komabe, anthu ena amene ndi amanyazi amakwanitsa kuuza ena zokhudza Baibulo n’kumasangalala ndi utumiki wawo. Kodi tingaphunzirepo chiyani pa chitsanzo chawo?

Onerani VIDIYO yakuti Ndimachita Zonse Zomwe Ndingathe Ngakhale Kuti Ndine Wamanyazi. Kenako funsani funso ili:

  • Kodi malangizo amene Mlongo Lee anauzidwa ndi agogo ake akuti “azichita zonse zomwe angathe potumikira Yehova” anamuthandiza bwanji?

Baibulo limasonyeza kuti Mose, Yeremiya komanso Timoteyo anali amanyazi. (Eks 3:11; 4:10; Yer 1:6-8; 1Ti 4:12) Komabe, iwo anakwanitsa kuchita zambiri potumikira Yehova chifukwa choti Yehovayo anali nawo. (Eks 4:12; Yer 20:11; 2Ti 1:6-8)

Zithunzi: 1. Mose wanyamula miyala iwiri yomwe panalembedwa Malamulo 10. 2. Yeremiya akupemphera. 3. Timoteyo akuwerenga mpukutu.

Werengani Yesaya 43:1, 2. Kenako funsani mafunso otsatirawa:

  • Kodi Yehova akulonjeza chiyani anthu amene amamulambira?

Kodi masiku ano Yehova angathandize bwanji anthu amene amachita manyazi kuti azikonda utumiki?

Onerani VIDIYO yakuti Mukabatizidwa Muzisangalala Kwambiri—Kachigawo Kake. Kenako funsani mafunso otsatirawa:

  • Kodi Mlongo Jackson anaona bwanji kuti Yehova ndi wamphamvu komanso amawathandiza pa utumiki wawo?

  • Kodi kulalikira kungathandize bwanji munthu amene ndi wamanyazi?

8. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) bt mutu 21 ¶8-13, bokosi patsamba 169

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 151 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena