Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yb16 tsamba 145
  • Tinapulumuka Chifukwa Chotsatira Malangizo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tinapulumuka Chifukwa Chotsatira Malangizo
  • Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2016
  • Nkhani Yofanana
  • “Wetani Gulu la Nkhosa za Mulungu Lomwe Analisiya M’manja Mwanu”
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Kodi Kuofesi ya Mboni za Yehova Kumachitika Zotani?
    Kodi Ndani Akuchita Chifuniro cha Yehova Masiku Ano?
  • Abusa, Tsanzirani Abusa Aakulu
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Poyamba Anali Mtsogoleri wa Zigawenga Koma Kenako Anakhala Nzika Yabwino
    Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2016
Onani Zambiri
Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2016
yb16 tsamba 145

INDONESIA

Tinapulumuka Chifukwa Chotsatira Malangizo

Blasius da Gomes

  • CHAKA CHOBADWA 1963

  • CHAKA CHOBATIZIDWA 1995

  • MBIRI YAKE Mkulu amene anasamalira nkhosa mwachikondi, pa nthawi imene panali mavuto a zachipembedzo mumzinda wa Ambon, womwe ndi mbali ya zilumba za Maluku.

M’bale Blasius da Gomes

PA 19 January 1999, Asilamu ndi Akhristu anayamba kumenyana koopsa chifukwa ankadana kwambiri. Maguluwa ankamenyana pa mtunda wa makilomita atatu kuchokera kumene ndinkakhala.a

Nditatsimikizira kuti banja langa ndi lotetezeka, ndinaimbira foni ofalitsa ena kuti ndidziwe mmene alili. Ndinawalimbikitsa kuti asachite mantha komanso kuti ayesetse kupewa kupita kumalo amene kunkachitika zachipolowezi. Kenako akulu anakalimbikitsa abale ndi alongo powauza mfundo za m’Malemba komanso anawalimbikitsa kuti azisonkhana m’timagulu.

A ku ofesi ya nthambi anatilimbikitsa kuti tiuze abale ndi alongo amene ankakhala m’madera omwe anthu ankamenyana kwambiri, kuti asamukeko. Tinauza mabanja angapo malangizo amenewa, koma m’bale wina amene sanamvere anaphedwa ndi gulu la anthu olusa. Aliyense amene anamvera malangizo ochokera ku ofesi ya nthambi anapulumuka.

a Kumenyanaku kunkachitika m’madera onse a ku Maluku ndipo kunatenga pafupifupi zaka ziwiri. Zipolowezi zinachititsa kuti anthu ambiri athawe m’nyumba zawo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena