Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mrt nkhani 14
  • Kodi Yohane M’batizi Anakhalapodi?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Yohane M’batizi Anakhalapodi?
  • Nkhani Zina
  • Nkhani Yofanana
  • Anaphedwa pa Tsiku Lokondwerera Kubadwa
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Kodi Yohane M’batizi Anali Ndani?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kupha Mwambanda pa Phwando la Tsiku Lakubadwa
    Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Kupha Munthu Mkati mwa Phwando Lokumbukira Tsiku Lobadwa
    Nsanja ya Olonda—1987
Onani Zambiri
Nkhani Zina
mrt nkhani 14
Yohane M’batizi akubatiza anthu.

Kodi Yohane M’batizi Anakhalapodi?

Nkhani za m’mabuku a Uthenga Wabwino zimatchula za munthu wina dzina lake Yohane M’batizi, yemwe ankalalikira za Ufumu wa Mulungu ku Yudeya. Kodi zimene Baibulo limanena za munthu ameneyu n’zoona? Taganizirani mfundo izi:

  • Baibulo limanena kuti: “Yohane M’batizi anapita m’chipululu cha Yudeya n’kuyamba kulalikira. Iye anali kulalikira kuti: ‘Lapani, pakuti ufumu wakumwamba wayandikira.’” (Mateyu 3:1, 2) Kodi zimene lembali limanena n’zogwirizana ndi zimene akatswiri olemba mbiri zakale anapeza? Inde.

    Katswiri wina wolemba mbiri yakale dzina lake Flavius Josephus anafotokoza za munthu wina dzina lake “Yohane M’batizi,” yemwe “ankalimbikitsa Ayuda kuti akhale olungama,” n’cholinga choti “adzipereke kwa Mulungu” komanso kuti “abatizidwe.”—Jewish Antiquities, Book XVIII.

  • Baibulo limanena kuti Yohane anadzudzula Herode Antipa, amene ankalamulira ku Galileya ndi ku Pereya. Herode anali Myuda yemwe ankaoneka kuti amatsatira Chilamulo. Yohane anadzudzula Herode chifukwa choti anakwatira Herodiya, mkazi wa m’bale wake. (Maliko 6:18) Akatswiri ena anafotokozaponso za nkhani imeneyi.

    Josephus, katswiri wolemba mbiri ananena kuti Antipa “anam’konda kwambiri Herodiya” ndipo “mopanda manyazi anamufunsira kuti amange naye banja.” Herodiya anavomera ndipo anasiya mwamuna wake n’kukwatirana ndi Antipa.

  • Baibulo limanenanso kuti “anthu ochokera ku Yerusalemu ndi ku Yudeya konse ndiponso ochokera m’midzi yonse yapafupi ndi Yorodano anali kubwera kwa iye [Yohane]. Iye anali kuwabatiza mumtsinje wa Yorodano.”—Mateyu 3:5, 6.

    Josephus anatsimikizira kuti zimenezi zinkachitikadi. Iye analemba kuti “khamu” la anthu linkabwera kudzaona Yohane ndipo “linkalimbikitsidwa komanso kukhudzidwa kwambiri ndi ulaliki wake.”

Apa n’zoonekeratu kuti Josephus, katswiri wolemba mbiri yakale, anatsimikizira mfundo yakuti Yohane M’batizi anakhalapodi. Ndipo ifenso tiyenera kukhulupirira zimenezi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena