Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g92 4/8 tsamba 30
  • Kodi Uchidakwa Uli Choloŵa?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Uchidakwa Uli Choloŵa?
  • Galamukani!—1992
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Majini Athu Amaikiratu Zamtsogolo Mwathu?
    Galamukani!—1996
  • Agogo “Atsopano”
    Galamukani!—1999
  • Mukhoza Kulaka Mavuto Owononga Banja
    Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
  • Kholo Chidakwa—Kodi Ndingalake Motani?
    Galamukani!—1992
Galamukani!—1992
g92 4/8 tsamba 30

Kodi Uchidakwa Uli Choloŵa?

Malinga ndi kufufuza kolembedwa mu The Journal of the American Medical Association, asayansi akulingalira kuti kwa anthu ena, chikhoterero cha kukhala zidakwa chingalandiridwe kudzera mwa jini inayake. Magaziniwo ananena kuti iwo apeza jini imene imaika anthu paupandu wakukhala zidakwa. Komabe, asayansi akuchenjeza kuti palibe jini imene imachititsa uchidakwa. Mkulu wa gulu lofufuzalo anati: “Ambuye wabwino sanapange jini yauchidakwa, koma imene imawoneka kukhala yoloŵetsedwa m’mikhalidwe yokonda zokondweretsa.”

Lipotilo linapitiriza kuti: “Ofufuza ananena kuti palibe jini iriyonse, kuphatikizapo imeneyo, imene inachititsapo mpangidwe uliwonse wa uchidakwa. Anthu ena okhala ndi jini yofufuzidwayo sanakhale zidakwa, pamene kuli kwakuti ena amene alibe jini imeneyi anakhala zidakwa . . . Zinthu zina za kakhalidwe ndi miyambo zimayambitsa vuto limeneli mwa zidakwa zambiri.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena