Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g00 6/8 tsamba 11
  • Pamene Nthenda Yaikulu Yagwira Banja

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pamene Nthenda Yaikulu Yagwira Banja
  • Galamukani!—2000
  • Nkhani Yofanana
  • Mmene Mabanja Amapiririra Matenda Aakulu
    Galamukani!—2000
  • Matenda Aakulu Ndi Nkhani ya Banja Lonse
    Galamukani!—2000
  • Kodi Baibulo Lingandithandize Kupirira Matenda?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Mulungu Akulitsa Mbewu ku Alaska
    Nsanja ya Olonda—1998
Onani Zambiri
Galamukani!—2000
g00 6/8 tsamba 11

Pamene Nthenda Yaikulu Yagwira Banja

CHIMWEMWE cha banja la a Du Toit n’chochititsa ena kukhala achimwemwe. N’zochititsa chidwi kwabasi kuona mmene amakonderana. Mutakumana nawo, simungaganize n’komwe zoti iwo apirira mavuto ambiri.

Choyamba, pamene mwana wawo wachisamba Michelle anali ndi zaka ziŵiri, Braam ndi Ann anauzidwa kuti iye ali ndi nthenda yaikulu yotengera mwachibadwa imene imafooketsa minofu.

Ann, yemwe ndi mayi ake a mtsikanayo anafotokoza kuti, “mwadzidzidzi, umayenera kuphunzira mmene ungachitire kuti upirire ndi nthenda yaikulu yofooketsayi. Umadziŵa kuti moyo wabanja zaterepa udzasintha kwambiri.”

Komabe atabereka mwana wina wamkazi ndi wamwamuna, vuto lowonjezereka linagweranso banjali. Tsiku lina ana atatuwo anali kuseŵera panja, kenako ana aakazi aŵiriwo anathamangira m’nyumba uku akulira. “Mayi! Mayi! Bwerani msanga. Neil sali bwino!”

Atatuluka, Ann anaona mutu wa Neil yemwe anali ndi zaka zitatu uli khoba! Iye anali kulephera kuudzutsa.

Ann akukumbukira kuti, “ndinangoti kakasi kusoŵa chochita, ndipo nthaŵi yomweyo ndinazindikira vutolo. Zinandiŵaŵa mumtima podziŵa kuti mwana wamng’ono wathanzi ngati ameneyu adzakhalanso ndi vuto lomwelo la nthenda yofooketsa minofu yomwe inagwira mlongo wake wamkulu.”

“Chisangalalo choti tayamba moyo wabanja tili athanzi, posakhalitsa chinaloŵedwa m’malo ndi mavuto osaneneka amene sitinakumanepo nawo n’kalelonse,” anatero a Braam womwe ndi bambo a m’banjali.

M’kupita kwanthaŵi Michelle, ngakhale kuti amalandira thandizo lamankhwala labwino koposa, anamwalira chifukwa cha matenda ena obwera chifukwa cha nthenda yakeyo. Panthaŵiyo n’kuti ali ndi zaka 14 zokha basi. Neil akupitirizabe kulimbana ndi mavuto a nthenda yakeyo.

Zimenezi zikubweretsa funso lakuti, Kodi mabanja onga ngati la a Du Toit angapirire motani mavuto okhala ndi banja la anthu odwala matenda aakulu? Kuti tiyankhe funso limeneli, tiyeni tione njira zina zimene matenda aakulu amakhudzira mabanja.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena