Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g01 5/8 tsamba 3
  • Ndende Zili Pamavuto Oopsa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ndende Zili Pamavuto Oopsa
  • Galamukani!—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Njira Yothetsera Vutolo Ndiyo Ikulikulitsanso?
    Galamukani!—2001
  • Kodi Zachiwawa Zingathetsedwe?
    Galamukani!—2008
  • “Kodi Akaidi Angatheke Kuwasintha?”
    Galamukani!—2005
  • Kodi Kusinthadi Ambanda N’kotheka?
    Galamukani!—2001
Onani Zambiri
Galamukani!—2001
g01 5/8 tsamba 3

Ndende Zili Pamavuto Oopsa

“Kumanga ndende zina pofuna kuchepetsa umbanda kuli ngati kutsegula manda ena pofuna kuchepetsa matenda oopsa,” anatero ROBERT GANGI, KATSWIRI WA ZANDENDE.

NTHAŴI zambiri m’madera mmene zinthu zina zosasangalatsa amazitchula mozungulira, anthu amatchula mawu ena omveka bwinopo akamatchula mawu osautsa akuti “ndende.” Anthu a m’madera ena akamatchula ndende amati “n’kumaphunziro” kumene anthu amaphunzirako “luso lantchito zosiyanasiyana” ndiponso kumene “amathandizidwa.” Anthu ena amakondanso kutchula mawu ena m’malo mwa mawu ochotsa ulemu akuti “mkaidi.” Komatu mukaonetsetsa mupeza kuti ndende zili ndi mavuto oopsa masiku ano. Pakufunika ndalama zambiri zosungira omangidwa ndiponso vuto lokwaniritsa cholinga chomanga anthu oswa lamulo likukulirakulira.

Anthu ena akukayikira ngati ndende zilidi zothandiza. Amati ngakhale kuti akaidi padziko lonse achuluka mpaka kuposa mamiliyoni asanu ndi atatu, upandu sunachepe n’komwe m’mayiko ambiri. Komanso, ngakhale kuti anthu ambiri amene ali m’ndende anamangidwira mankhwala osokoneza bongo, mankhwalawo akupezekabe modetsa nkhaŵa m’madera ena.

Komabe, anthu osiyanasiyana amaona kuti kumangidwa ndi chibalo chochita kuchifuna. Munthu wolakwa akamangidwa, iwo amaona kuti pachitika chilungamo. Mtolankhani wina anafotokoza khalidwe lokonda kumangomangamanga anthu olakwa kuti lakhala ngati “matenda.”

Pali zifukwa zikuluzikulu zinayi zimene ophwanya malamulo amawaikira m’ndende: (1) Kuwalanga, (2) kuteteza anthu, (3) kuletsa umbanda winanso, ndiponso (4) kusintha khalidwe la olakwawo, powaphunzitsa kuti akadzawamasula adzakhale osunga malamulo ndiponso othandiza ena. Tiyeni tione ngati ndende zikukwaniritsadi zolinga zimenezi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena