Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g02 9/8 tsamba 15
  • Kugwiritsa Ntchito Galamukani! Mwanjira Yabwino

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kugwiritsa Ntchito Galamukani! Mwanjira Yabwino
  • Galamukani!—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Chikundiletsa Kubatizidwa N’chiyani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Mulungu Akulitsa Mbewu ku Alaska
    Nsanja ya Olonda—1998
  • Munthu Amene Mumamukonda Akamwalira
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2019
  • “Ndinkaona, Koma Sindinkadziwa Tanthauzo Lake”
    Nsanja ya Olonda—2013
Onani Zambiri
Galamukani!—2002
g02 9/8 tsamba 15

Kugwiritsa Ntchito Galamukani! Mwanjira Yabwino

ALI ndi zaka 16, mtsikana wina wa ku United States, dzina lake Vanessa, yemwe ali m’gulu la Mboni za Yehova, anauzidwa kuti alembe lipoti la kusukulu lokhudza matenda enaake om’lepheretsa munthu kukonda zakudya. Iye anati: “Ndinafufuza m’mabuku osiyanasiyana, koma ndinangopezamo nkhani zochepa chabe. Ndinawauza makolo anga za nkhani imeneyi, ndipo iwo anandiuza kuti ndiifufuze m’mabuku athu.”

Atafufuza m’mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova, Vanessa anapeza zinthu zambiri zoti alembe m’lipoti lakelo. Iye anati: “Komatu imeneyi inali mbali yochepa chabe ya ntchito imene anatipatsayo. Nditatha zonsezi, ndinafunikanso kuti ndikakambe zimene ndinapeza pamaso pa aphunzitsi athu ndi ophunzira anzanga okwana 20!” Kodi Vanessayo anatha bwanji kuchita chintchito chovutachi?

Monga mmene amachitira a Mboni za Yehova padziko lonse, Vanessa amaphunzira kulankhula pagulu m’Sukulu ya Utumiki wa Teokalase imene imachitikira pa Nyumba ya Ufumu ya kufupi ndi kwawo. Vanessayo anati: “Chifukwa cha sukulu imeneyi timakhala okonzeka mokwanira kupita kukatumikira ndiponso kukalankhula ndi anthu ena. Amatilangizanso zimene tiyenera kuchita kuti anthu amve bwinobwino zimene tikuwauza.” Ndiye kodi Vanessa anakhoza bwanji pa mayeso atachita khama chonchi? Iye anati: “Ndinapambana kuposa ena onse.”

Vanessa ali m’gulu la achinyamata ambiri amene akugwiritsa ntchito bwino kwambiri mabuku ozikidwa pa Baibulo ndiponso maphunziro ena auzimu. Tiyenera kuwayamikira kwambiri achinyamata otereŵa chifukwa chakuti akumvera mawu olimbikitsa a pa Mlaliki 12:1, amene amati: “Ukumbukirenso Mlengi wako masiku a unyamata wako.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena