Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g03 12/8 tsamba 16
  • Anthu Amatengera Mmene Mlengi Analengera Zinthu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Anthu Amatengera Mmene Mlengi Analengera Zinthu
  • Galamukani!—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Dzira
    Galamukani!—2011
  • Mungakonze Mphamvu Yanu ya Kukumbukira
    Galamukani!—1996
  • Chilengedwe Chimatiphunzitsa Zambiri
    Galamukani!—2010
Galamukani!—2003
g03 12/8 tsamba 16

Anthu Amatengera Mmene Mlengi Analengera Zinthu

Kodi zimatheka bwanji kuti magolobo a magetsi omwe ndi opyapyala kwambiri asamaphwanyike powakanikiza kuti alowe moikamo magolobo? Malinga ndi zimene linanena buku lotchedwa How in the World?, yankho lake ndi mmene golobolo linapangidwira, limene anatengera “mmene dzira linapangidwira.” Ngakhale kuti chakunja cha dzira n’chopyapyala kwambiri, mazira saphwanyika ndi kulemera kwa mbalame ikamakhalira. Zimenezi zili choncho chifukwa mmene dzira linapangidwira limakhala lamphamvu moti silingaphwanyike. (Chakunja cha dzira chochindikala chingalepheretse kamwana kuti katuluke m’dzira.) Potengera mmene Mlengi analengera zinthu, magolobo ndi ozungulira moti akakanikizidwa, “sapanikizika malo amodzi okha koma kukanikizako kumapita mbali zonse za golobolo.” Choncho, monga mmene zilili ndi dzira, kukanikiza kwamphamvu sikukhala malo amodzi, ndipo golobo siliphwanyika. Anthu adziŵa zambiri pophunzira chilengedwe!

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena