Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 8/07 tsamba 3
  • Pezani Malangizo Abwino

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pezani Malangizo Abwino
  • Galamukani!—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Malangizo a Akatswiri Amasinthasintha
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Malangizo Odalirika Olerera Ana
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Mungatani Kuti Banja Lanu Likhale Losangalala?​—Mbali Yachiwiri
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Phunzitsani Mwana Wanu Kuyambira Paukhanda Wake
    Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
Onani Zambiri
Galamukani!—2007
g 8/07 tsamba 3

Mfundo 1

Pezani Malangizo Abwino

N’chifukwa chiyani? Makolo ena akanyamula mwana wawo wakhanda m’manja kwa nthawi yoyamba, amakhala ndi nkhawa yaikulu. Bambo wina wa ku Britain, dzina lake Brett anati: “Ndinali wosangalala kwambiri moti ndinkangoona ngati kutulo. Koma ndinalinso ndi nkhawa yaikulu poganizira za udindo umenewu, ndipo ndinkaopa kuti mwina sinditha kuukwanitsa.” Mayi wina wa ku Argentina, dzina lake Monica, anati: “Ndinkada nkhawa kwambiri poganizira kuti mwina sinditha kusamalira bwino mwana wanga. Ndinkadzifunsa kuti: ‘Kodi nditha kumulera bwinobwino kuti adzakhale munthu wodalirika?’”

Kodi mukutha kumvetsa chimwemwe komanso nkhawa imene makolo amenewa anali nayo? Inde, kulera mwana ndi imodzi mwa ntchito zovuta koma zosangalatsa zedi. Monga bambo wina ananenera, “muli ndi mwayi umodzi wokha wolera mwana wanu bwino.” Popeza kuti makolo angathandize kwambiri kuti ana akhale athanzi ndiponso osangalala, mungaone kuti mukufunikadi malangizo odalirika a mmene mungakwaniritsire bwino udindo wanu.

Kuvuta kwake: Zimaoneka kuti aliyense ali ndi malangizo pankhani ya kaleredwe ka ana. Kale anthu akakhala ndi mwana woyamba, ankadalira chitsanzo cha makolo awo kapena malangizo a chipembedzo chawo. Koma m’mayiko ambiri, mabanja sakuyenda bwino ndipo anthu ambiri asiya kutsatira zachipembedzo. Motero, makolo ambiri amafunsira malangizo kwa akatswiri odziwa za kulera ana. Zina mwa zinthu zimene akatswiri amenewa amanena n’zomveka ndithu. Koma nthawi zina malangizowa amakhala otsutsana ndipo sachedwa kutha ntchito.

Mmene mungakwanitsire: Funani malangizo kwa munthu amene amadziwa bwino kwambiri za kulera ana. Iyeyu ndi Mlengi wa anthu, Yehova Mulungu. (Machitidwe 17:26-28) Mawu ake Baibulo, ali ndi malangizo osapita m’mbali ndiponso zitsanzo zimene zingakuthandizeni kulera bwino ana anu. Iye analonjeza kuti: “Ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo.”—Salmo 32:8.

Kodi Mulungu amapereka malangizo otani kwa makolo, amene angawathandize kulera ana awo kuti adzakhale osangalala?

[Mawu Otsindika patsamba 3]

“Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako.”—Miyambo 3:5

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena