Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 3/14 tsamba 16
  • Khungu la Njoka

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Khungu la Njoka
  • Galamukani!—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Tetezani Khungu Lanu
    Galamukani!—2005
  • Njoka Yamkuwa
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Anthu Akhala Akulambira Njoka kwa Zaka Zambiri
    Galamukani!—2010
  • Zamkatimu
    Galamukani!—2005
Onani Zambiri
Galamukani!—2014
g 3/14 tsamba 16
Njoka ikukwera mumtengo

KODI ZINANGOCHITIKA ZOKHA?

Khungu la Njoka

CHIFUKWA choti njoka imagwiritsa ntchito mimba poyenda, khungu lake limafunika kukhala lolimba kuti lisamanyuke chisawawa. Njoka zina zimatha kukwera mitengo yaminga, ndipo zina zimayenda pamchenga ukuluukulu. Kodi n’chiyani chimapangitsa kuti khungu la njoka likhale lolimba chonchi?

Taganizirani izi: Khungu la njoka limasiyana kukhuthala komanso maonekedwe ake malinga ndi mtundu wa njokayo. Komabe njoka zonse zimakhala ndi khungu lolimba pamwamba ndipo mkati mwake limakhala lofewa. Kodi zimenezi zimathandiza bwanji? Katswiri wina wofufuza zinthu, dzina lake Marie-Christin Klein, ananena kuti: “Chinthu chimene chimakhala ndi khungu lolimba pamwamba koma n’kukhala lofewa mkati mwake, chikakhulika ndi chinachake sichivulala kwambiri.” Mmene khungu la njoka linapangidwira, zimathandiza kuti ikamayenda isamavulale kwambiri ndi zinthu monga miyala yakuthwa. N’zofunikadi kuti khungu la njoka likhale lolimba chonchi chifukwa nthawi zambiri pamatenga miyezi iwiri kapena itatu kuti njoka ifundule.

Zinthu zopangidwa kuchokera ku khungu la njoka zingathandize pa nkhani ya zachipatala. Mwachitsanzo, zingathandize popanga zinthu zolimba komanso zosaterera zimene zingathe kuikidwa m’thupi la munthu ngati ziwalo zake kapena zinthu zina zasiya kugwira ntchito bwino. Komanso kupanga makina akuluakulu otengera mmene khungu la njoka limakhalira kungathandize kuti makinawo asamawononge kwambiri chilengedwe.

Kodi inuyo mukuganiza bwanji? Kodi zinangochitika zokha kuti khungu la njoka likhale lolimba chonchi, kapena pali winawake amene analilenga?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena