Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 7/15 tsamba 7
  • Kodi Mumatani Mukakumana ndi Mavuto?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mumatani Mukakumana ndi Mavuto?
  • Galamukani!—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Vuto Limene Limakhalapo: Zinthu Zina Simungazisinthe
    Galamukani!—2015
  • Vuto Limene Limakhalapo: Kukhala Wosasangalala
    Galamukani!—2015
  • Kodi Munayamba Mwadzifunsapo?
    Galamukani!—2019
  • Dziko Latsopano—Kodi Mudzakhalamo?
    Nsanja ya Olonda—2000
Onani Zambiri
Galamukani!—2015
g 7/15 tsamba 7

NKHANI YA PACHIKUTO | KODI MUMATANI MUKAKUMANA NDI MAVUTO?

Musataye Mtima Mukakumana ndi Mavuto

Munthu akuyendetsa boti mtima uli m’malo

ANTHU ambiri amakonda kunena kuti, Pendapenda si kugwa. Choncho tisamataye mtima ngati penapake sizikutiyendera bwino. Masiku ano aliyense amakumana ndi mavuto. Koma chofunika n’kuvomereza mavutowo kenako n’kuona zimene tingakwanitse kuchita. N’zoona kuti mavuto ena akhoza kusintha koma kusintha kwenikweni kudzachitika m’dziko latsopano.

Baibulo limasonyeza kuti ikubwera nthawi pamene moyo wathu uzidzayenda bwinobwino. Tidzatha kuchita zonse zimene tikufuna popanda mavuto, kupanikizika kapena kukhumudwa. (Yesaya 65:21, 22) Baibulo limati umenewu udzakhala “moyo weniweniwo.”—1 Timoteyo 6:19.

“Iwo adzamanga nyumba n’kukhalamo. Adzabzala minda ya mpesa n’kudya zipatso zake. Sadzamanga wina n’kukhalamo. Sadzabzala wina n’kudya. Pakuti masiku a anthu anga adzakhala ngati masiku a mtengo, ndipo anthu anga osankhidwa mwapadera adzapindula mokwanira ndi ntchito ya manja awo.”—Yesaya 65:21, 22.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena