Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g19 No. 3 tsamba 3
  • Buku Lakale Lokhala ndi Mfundo Zothandiza Masiku Ano

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Buku Lakale Lokhala ndi Mfundo Zothandiza Masiku Ano
  • Galamukani!—2019
  • Nkhani Yofanana
  • Zimene Zili M’magaziniyi: Baibulo Lingakuthandizeni Kukhala ndi Moyo Wabwino Kwambiri
    Galamukani!—2019
  • Zimene Zili M’Magaziniyi
    Galamukani!—2019
  • Buku Lothandiza pa Moyo Wamakono
    Buku la Anthu Onse
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kudalira Baibulo Kuti Lizititsogolera?
    Galamukani!—2006
Onani Zambiri
Galamukani!—2019
g19 No. 3 tsamba 3
Bambo akuona Mabaibulo akale kumiziyamu

Buku Lakale Lokhala ndi Mfundo Zothandiza Masiku Ano

Anthu ambiri amaona kuti Baibulo ndi buku lofunika kwambiri pa nkhani zachipembedzo. Komabe, si kuti ndi lothandiza pa nkhani zachipembedzo zokha. Lilinso ndi malangizo othandiza pa mbali zonse za moyo wathu.

Mwachitsanzo, taonani zimene ena ananena pa nkhani ya mmene kuphunzira ndi kugwiritsa ntchito mfundo za m’Baibulo kwawathandizira kuti akhale ndi moyo wabwino.

“Ndimaona kuti ndili ndi mtendere wamumtima. Sindivutika kwambiri ndi nkhawa moti ndimakhala wosangalala.”​—Fiona.

“Kuphunzira Baibulo kwandithandiza kudziwa chifukwa chake ndili ndi moyo.”​—Gnitko.

“Panopo ndili ndi moyo wabwino kwambiri. Ndimapeza nthawi yocheza ndi banja langa ndipo sindikhalanso ndi moyo wongodzipanikiza ndi ntchito.”​—Andrew.

Palinso anthu ambiri padziko lonse omwe amavomereza kuti mfundo za m’Baibulo zimawathandiza pamoyo wawo.

Tsopano tiyeni tione mmene Baibulo lingatithandizire . . .

  • Kukhala ndi moyo wathanzi

  • Kukhala ndi mtendere wa m’maganizo

  • Kukhala ndi banja komanso mabwenzi abwino

  • Kugwiritsa ntchito bwino ndalama

  • Kukhala pa ubwenzi ndi Mulungu

Magaziniyi ikuthandizani kuona kuti Baibulo si buku lothandiza pa nkhani zachipembedzo zokha, koma lingakuthandizeninso pamoyo wanu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena