Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g22 No. 1 tsamba 7-9
  • 2 | Muzisamala Ndalama

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • 2 | Muzisamala Ndalama
  • Galamukani!—2022
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • CHIFUKWA CHAKE ZILI ZOFUNIKA
  • Zimene Muyenera Kudziwa
  • Zimene Mungachite Panopa
  • Zimene Mungachite Ngati Mukupeza Ndalama Zochepa
    Nkhani Zina
  • Mmene Mungapeŵere Kukhala m’Ngongole
    Galamukani!—1997
  • Muzigwiritsa Ntchito Ndalama Mwanzeru
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Zimene Mungachite Ngati Muli Ndi Ngongole
    Nsanja ya Olonda—2012
Onani Zambiri
Galamukani!—2022
g22 No. 1 tsamba 7-9
Kalipentala akukhoma msomali pa thabwa.

MAVUTO A M’DZIKOLI

2 | Muzisamala Ndalama

CHIFUKWA CHAKE ZILI ZOFUNIKA

Tsiku lililonse, anthu ambiri amavutika kuti apeze zinthu zofunika pa moyo. N’zomvetsa chisoni kuti mavuto a m’dzikoli angawachititse kuti azivutika kwambiri. Chifukwa chiyani?

  • Kukakhala mavuto, zinthu monga zakudya komanso nyumba zimakhala zodula kwambiri.

  • Mavuto akachuluka, anthu ambiri amachotsedwa ntchito kapenanso malipiro amachepetsedwa.

  • Kukachitika ngozi zam’chilengedwe, mabizinesi amasokonekera komanso nyumba ndi katundu wina amawonongeka, ndipo zimenezi zimachititsa kuti anthu akhale pa umphawi.

Zimene Muyenera Kudziwa

  • Mukamagwiritsa ntchito bwino ndalama, sizingadzakuvuteni mukadzakumana ndi mavuto.

  • Kupeza ndalama zambiri, kusunga ndalama komanso kukhala ndi katundu wambiri, nthawi zina n’kosadalirika chifukwa zimatha mphamvu.

  • Pali zinthu zina zimene ndalama sizingagule monga kukhala wosangalala komanso kukhala ndi banja logwirizana.

Zimene Mungachite Panopa

Baibulo limanena kuti: “Pokhala ndi chakudya, zovala ndi pogona, tikhale okhutira ndi zinthu zimenezi.”​—1 Timoteyo 6:8.

Kukhala wokhutira kumaphatikizapo kudziikira malire pa zimene tikufuna, n’kumakhala wokhutira ndi zimene timafunikiradi tsiku ndi tsiku. Zimenezi n’zofunika kwambiri makamaka tikakhala kuti tikukumana ndi mavuto azachuma.

Kuti mukhale okhutira mumafunika kusintha zimene mumachita pa moyo wanu. Mukamafuna kukhala moyo wapamwamba woposa ndalama zimene mumapeza, mavuto anu azachuma sangathe.

KODI MUNGATANI KUTI MUPIRIRE?​—Mfundo Zimene Zingakuthandizeni

Pa nthawi yamavuto mungasamale ndalama zanu pogwiritsa ntchito njira zimenezi

MUZICHEPETSA ZINTHU ZIMENE MUMAGULA

  • Mayi wachikulire akuzula karoti pa dimba lake.

    Muzichepetsa zinthu zimene mumagula

    Musamapupulume kugula zipangizo kapena zovala ­zatsopano. Muzidzifunsa kuti: ‘Kodi ndikufunikiradi galimoto? Kodi ndingalime dimba la masamba?’

  • Musanagule chinthu muzidzifunsa kuti: ‘Kodi ndichofunikiradi? Kodi ndikwanitsa kugula?’

  • Ngati kwanu zimachitika, mungalembetse kuboma ­kapena ku mabungwe kuti muzilandira chithandizo.

“Monga banja, tinakhala pansi n’kuonanso mmene timagwiritsira ntchito ndalama. Tinachepetsa ndalama zimene timagwiritsa ntchito pochitira zosangalatsa. Tinayambanso kukonza chakudya chosawononga ndalama zambiri.”​—Gift.

MUZIPANGA BAJETI

Mayi akuwerengetsera zinthu zimene zili pa lisiti.

Muzipanga bajeti

Baibulo limanena kuti: “Zolinga za munthu wakhama zimam’pindulira, koma aliyense wopupuluma, ndithu adzasauka.” (Miyambo 21:5) Kupanga bajeti kumakuthandizani kuti musamawononge ndalama zambiri kuposa zimene mumapeza.

  • Choyamba, lembani ndalama zimene mupeze mwezi umenewo.

  • Chachiwiri, onani zinthu zimene mumafunika kulipira mwezi uliwonse.

  • Kenako yerekezerani zimene mumapeza ndi zimene mumagwiritsa ntchito, ndipo ngati n’zotheka mungachepetse kapena kuchotsa zina kuti zigwirizane ndi zimene mumapeza.

“Mwezi uliwonse timalemba ndalama zimene timapeza komanso zimene tikufunika kugwiritsa ntchito. Timayesetsa kusunga ndalama zogwiritsa ntchito pa zinthu zadzidzidzi komanso za zinthu zimene tikufuna kudzagula m’tsogolo. Tikamachita zimenezi sitikhala ndi nkhawa, chifukwa timadziwiratu mmene tingagwiritsire ntchito ndalama zimene timapeza.”​—Carlos.

MUZIPEWA NGONGOLE / MUZISUNGA NDALAMA

  • Mayi akuthandiza mwana wake wamkazi kuika ndalama m’botolo.

    Muzipewa ngongole / muzisunga ndalama

    Muzikhala ndi pulani yabwino kuti mubweze ngongole zimene muli nazo. Ngati n’kotheka, musamakongole ndalama n’komwe. M’malomwake muziyesetsa kusunga ndalama kuti mugule zimene mukufuna.

  • Mwezi uliwonse muzisunga kandalama koti mudza­gwiritse ntchito pa zinthu zimene mukudziwiratu kapena zadzidzidzi.

MUZILIMBIKIRA NTCHITO

Baibulo limanena kuti: “Kugwira ntchito iliyonse kumapindulitsa.”​—Miyambo 14:23.

  • Kalipentala akukhoma msomali pa thabwa.

    Muzilimbikira ntchito

    Muziona ntchito yanu moyenera. Ngakhale itakhala kuti si imene munkafuna, komabe imakupatsani ndalama.

  • Muziyesetsa kugwira ntchito mwakhama komanso muzikhala odalirika. Zimenezi zidzakuthandizani kuti mukhalebe pa ntchitoyo, komabe ngati ingathe, simudzavutika kupeza ina m’tsogolo.

“Ndimagwira ntchito iliyonse imene yapezeka, ngakhale ntchito yake si imene ndimafuna kapena ndalama zake ndi zochepa. Ndimayesetsa kukhala wodalirika komanso kugwira bwino ntchito ngati kuti ntchitoyo ndi yanga.”​—Dmitriy.

Ngati mukufuna ntchito . . .

  • Muzichitapo kanthu. Muzifunsira ntchito ku maka­mpani amene kungakhale ntchito zimene mungagwire ngakhale sanalengeze kuti akufuna anthu antchito. Muziuza anzanu komanso achibale kuti mukufunafuna ntchito.

  • Muzikhala okonzeka kusintha. N’zovuta kuti mungapeze ntchito yomwe ili ndi zonse zimene mumafuna.

Makolo akupanga bajeti ndipo ana awo akusewera cha pafupi.

DZIWANI ZAMBIRI. Werengani nkhani yakuti “Zimene mungachite ngati mukupeza ndalama zochepa.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena