Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g22 No. 1 tsamba 10-12
  • 3 | Muziteteza Ubwenzi Wanu ndi Anzanu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • 3 | Muziteteza Ubwenzi Wanu ndi Anzanu
  • Galamukani!—2022
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • CHIFUKWA CHAKE ZILI ZOFUNIKA
  • Zimene Muyenera Kudziwa
  • Zimene Mungachite Panopa
  • Pali Anzanu Abwino ndi Anzanu Oipa
    Galamukani!—2004
  • Muzisankha Mwanzeru Anthu Ocheza Nawo
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Kupeza Anzathu Omwe Timalakalaka
    Galamukani!—2004
  • Mungathe Kukhalabe ndi Mabwenzi M’dziko Lopanda Chikondi Lino
    Nsanja ya Olonda—2009
Onani Zambiri
Galamukani!—2022
g22 No. 1 tsamba 10-12
Banja lachikulire likuhagana.

MAVUTO A M’DZIKOLI

3 | Muziteteza Ubwenzi Wanu ndi Anzanu

CHIFUKWA CHAKE ZILI ZOFUNIKA

Mavuto a m’dzikoli akumachititsa kuti anthu ambiri azikhala ndi nkhawa. Chifukwa cha zimenezi, mosadziwa, anthu ena akumachita zinthu zosonyeza kuti sakonda anzawo.

  • Anthu ena amadzipatula kuti azichita zinthu paokha.

  • Anthu ena apabanja sakumachedwa kuyambana.

  • Chidwi cha makolo ena pa ana awo chachepa, pomwe ena sakumaganizira n’komwe nkhawa zimene ana awo amakhala nazo.

Zimene Muyenera Kudziwa

  • Kukhala ndi anzathu n’kwabwino, chifukwa amatithandiza kukhala ndi moyo wabwino komanso amatilimbikitsa makamaka pa nthawi imene takumana ndi mavuto.

  • Nkhawa zimene zimabwera chifukwa cha mavuto a m’dzikoli, zingachititse kuti musamagwirizane m’banja mwanu m’njira zimene simunkaziganizira.

  • Ana anu akamamvetsera pa wailesi kapena kuonera nkhani zoopsa pa TV, zingawasokoneze kwambiri.

Zimene Mungachite Panopa

Baibulo limanena kuti: “Bwenzi lenileni limakukonda nthawi zonse, ndipo bwenzilo ndi m’bale amene anabadwira kuti akuthandize pakagwa mavuto.”​—Miyambo 17:17.

Ganizirani za munthu amene angakuthandizeni komanso amene angakupatseni malangizo othandiza kenako m’pempheni. Kudziwa kuti winawake amakuganizirani kungakulimbikitseni kupirira mavuto amene mumakumana nawo.

KODI MUNGATANI KUTI MUPIRIRE?​—Mfundo Zimene Zingakuthandizeni

Pa nthawi ya mavuto mungateteze ubwenzi wanu pochita zotsatirazi

MUZILIMBITSA BANJA LANU

Banja lachikulire likuhagana.

Muzilimbitsa banja lanu

Baibulo limanena kuti: “Awiri amaposa mmodzi . . . Ngati mmodzi wa iwo atagwa, winayo akhoza kum’dzutsa mnzakeyo.” (Mlaliki 4:9, 10) Anthu okwatirana ayenera kumachita zinthu ngati anthu awiri oyendetsa ndege imodzi omwe amakhala ndi cholinga chimodzi, osati ngati ali mundege ziwiri zosiyana zomwe zikufuna kuphulitsana

  • Muziyesetsa kuti musamachitire chipongwe mkazi kapena mwamuna wanu, chifukwa cha mavuto amene mukukumana nawo. Ndipo muzikhala oleza mtima komanso ololera.

  • Mwina kamodzi pa wiki, muzikambirana ndi mkazi kapena mwamuna wanu za mavuto amene mukuyenera kuwakonza. Cholinga chanu chiyenera kukhala cholimbana ndi vutolo, osati kulimbana nokhanokha.

  • Muzipeza nthawi yochitira zinthu limodzi zimene nonse mumakonda..

  • Muzikumbukira nthawi yosangalatsa imene munkachitira zinthu limodzi, mwachitsanzo mungaone limodzi zithunzi za pa ukwati wanu.

“Anthu okwatirana sangamagwirizane pa chilichonse, koma zimenezi sizikutanthauza kuti sangamachitire zinthu limodzi. Iwo akhoza kusankha limodzi zochita kenako n’kuthandizana kuti akwaniritse zimene asankhazo.”​—David.

MUZILIMBITSA UBWENZI WANU NDI ANZANU

  • Azimayi a mitundu yosiyanasiyana akucheza limodzi mosangalala.

    Muzilimbitsa ubwenzi wanu ndi anzanu

    Kuwonjezera pa kulandira thandizo kuchokera kwa anzanu, muziganizira mmene inuyo mungawathandizire. Mukamalimbikitsa ena, inunso mumalimbikitsidwa.

  • Tsiku lililonse muziimbira foni kapena kulembera mameseji anzanu kuti mudziwe mmene zinthu zilili pa moyo wawo.

  • Muzifunsa anzanu mmene akukwanitsira kupirira mavuto ofanana ndi amene inunso mukukumana nawo.

“Mukakumana ndi mavuto aakulu, anzanu angakuthandizeni. Iwo angakuthandizeni kudziwa zochita ngakhale atangokukumbutsani zimene mukudziwa kale. Anzanu amakuganizirani, ndipo iwonso amadziwa kuti mumawaganizira.”​—Nicole.

MUZIKHALA KHOLO LOTHANDIZA

Makolo akhala padoko ndi ana awo awiri ndipo akusangalala ndi chilengedwe chokongola.

Muzikhala kholo lothandiza

Baibulo limanena kuti: “Munthu aliyense akhale wofulumira kumva, wodekha polankhula.” (Yakobo 1:19) Poyamba, ana anu angamavutike kukufotokozerani zinthu zimene zikuwadetsa nkhawa ndiponso zimene akuganiza, koma mukamawamvetsera mwatcheru, akhoza kumasuka ndi kukufotokozerani.

  • Muzipeza malo komanso mpata wabwino kuti ana anu amasuke kufotokoza zimene zikuwadetsa nkhawa. Ana ena amaona kuti amamasuka kufotokoza zamumtima mwawo akakhala m’galimoto, akamayenda, kapena akamadya limodzi ndi makolo awo osati akakhala pansi n’kumayang’anizana nawo.

  • Muzionetsetsa kuti ana anu asamaonere kwambiri nkhani zoopsa.

  • Muzithandiza ana anu kudziwa zimene banja lanu lakonza kuti mukhale otetezeka.

  • Muzidziwiratu zimene mungachite ngati patachitika zinthu zadzidzidzi, ndipo muziyeserera kuchita zimenezo ndi ana anu.

“Muzilankhula ndi ana anu ndipo muziwalola kuti afo­tokoze mmene akumvera. Akhoza kumadzibisa kuti asaoneke kuti ali ndi mantha, nkhawa kapenanso akwiya. Muziwauza ana anu kuti nthawi zina inunso mumamva choncho, ndiponso muziwauza zimene mumachita kuti muyambe kumva bwino.”​—Bethany.

Chithunzi cha muvidiyo yakuti “Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala.” Mwamuna ndi mkazi wake akuyenda mosangalala atagwirana manja.

DZIWANI ZAMBIRI. Onerani vidiyo yakuti Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena