Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 1
  • Mulungu Ayamba Kupanga Zinthu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mulungu Ayamba Kupanga Zinthu
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Mulungu Analenga Kumwamba ndi Dziko Lapansi
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Kodi Dzuwa ndi Mapulaneti Olizungulira Zinakhalako Bwanji?
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Kodi Mulungu Anayamba Liti Kulenga Zinthu?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Amene Anapanga Zinthu Zonse
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 1

NKHANI 1

Mulungu Ayamba Kupanga Zinthu

ZINTHU zabwino zimene tiri nazo zachokera kwa Mulungu. Iye anapanga dzuwa lidziunikira masana, ndi mwezi ndi nyenyezi kuti tikhale ndi kuunika usiku. Ndipo Mulungu anapanga dziko lapansi kuti tikhalepo.

Koma dzuwa, mwezi, nyenyezi ndi dziko lapansi sizinali zoyamba kupangidwa ndi Mulungu. Kodi mukudziwa choyamba? Mulungu anayamba kupanga anthu onga iye. Sitingaone anthu’wa, monga momwe sitingaonere Mulungu. M’Baibulo amene’wa amachedwa angelo. Mulungu anapanga angelo kukhala naye kumwamba.

Mngelo woyamba kupangidwa ndi Mulungu anali wapadera kwambiri. Ndiye Mwana woyamba wa Mulungu, ndipo anagwira ntchito ndi Atate wake. Anathandiza Mulungu kupanga dzuwa, mwezi, nyenyezi ndipo’nso dziko lathu lapansi.

Kodi dziko lapansi linali lotani pa nthawi’yo? Poyamba palibe akanakhala pa dziko lapansi. Panalibe kanthu kusiyapo chinyanja pa mtunda wonse. Koma Mulungu anafuna kuti anthu akhalepo. Chotero anayamba kutikonzera zinthu. Kodi anachitanji?

Eya, choyamba dziko’lo linafunikira kuunika. Chotero Mulungu anachititsa kuunika kuchokera ku dzuwa kuwalira dziko. Anapanga kuti pakhale usiku ndi usana. Kenako Mulungu anapangitsa mtunda kutundumuka pa madzi a nyanja’wo.

Poyamba panalibe kanthu pa mtundapo. Panali ngati chithunzi mukuona apa’chi. Panalibe maluwa, mitengo kapena zinyama. Munalibe ngakhale nsomba m’nyanjamo. Mulungu anali ndi ntchito yoti achite yochuluka kupanga dziko lapansi labwino’di kwa zinyama ndi anthu kukhalapo.

Yeremiya 10:12; Akolose 1:15-17; Genesis 1:1-10.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena