Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 3
  • Mwamuna ndi Mkazi Oyamba

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mwamuna ndi Mkazi Oyamba
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Mulungu Analenga Anthu Awiri Oyamba
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Mdani Wathu Womalizira Adzawonongedwa
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Adamu ndi Hava
    Kukambitsirana za m’Malemba
  • Ngati Adamu Anali Wangwiro, Kodi Zinatheka Bwanji Kuti Achimwe?
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 3

NKHANI 3

Mwamuna ndi Mkazi Oyamba

KODI chosiyana n’chiani m’chithunzi’chi? Ndicho anthu’wo. Ndiwo mwamuna ndi mkazo oyamba. Kodi anawapanga ndani? Ndiye Mulungu. Kodi mukudziwa dzina Lake? Ndiro Yehova. Ndipo iwo anachedwa Adamu ndi Hava.

Yehova anapanga Adamu motere. Anatenga dothi lapansi naumba nalo thupi langwiro, la munthu wamwamuna. Anauzira mpweya m’mphuno mwake, Adamu nakhala wamoyo.

Yehova anali ndi ntchito yoti Adamu achite. Anauza Adamu kucha maina zinyama zonse. Adamu angakhale atapenda zinyama’zo kwa nthawi yaitali kuti azisankhire maina abwino kwambiri. Pocha maina zinyama’zo iye anayamba kuona kanthu kena. Kotani?

Zinyama zonse zinali ziwiriziwiri. Panali njobvu zamphongo ndi zazikazi, mikango yamphongo ndi yaikazi. Koma Adamu analibe mnzake. Chotero Yehova anam’goneka tulo tatikulu, nachotsa nthiti yake imodzi. Nthiti’yo Yehova anaipanga mkazi wa Adamu.

Ha, ndi wokondwa chotani m’mene analiri Adamu tsopano! Ganizani m’mene Hava anakondwera kuikidwa m’munda wokongola’wo! Tsopano akanatha kubala ana ndi kukhala pamodzi mwachimwemwe.

Yehova anafuna kuti iwo akhale ndi moyo kosatha. Anafuna kuti iwo akongoletse dziko lonse ngati munda wa Edene’wo. Ha, ndi okondwera nawo chotani nanga m’mene analiri Adamu ndi Hava! Kodi mukanakonda kukongoletsa nawo dziko lapansi? Koma chimwemwe chao sichinakhalitse. Tiyeni tione chifukwa chake.

Salmo 83:18; Genesis 1:26-31; 2:7-25.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena