Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 7
  • Munthu Olimba Mtima

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Munthu Olimba Mtima
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • ‘Mulungu Anakondwera Naye’
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
  • Enoke Wopanda Mantha Zivute Zitani
    Nsanja ya Olonda—1997
  • Enoke Anayenda ndi Mulungu M’dziko la Anthu Osapembedza
    Nsanja ya Olonda—2001
  • Yendani ndi Mulungu M’nthawi ya Chipwirikiti Ino
    Nsanja ya Olonda—2005
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 7

NKHANI 7

Munthu Olimba Mtima

PAMENE anthu anayamba kuchuluka pa dziko, ambiri anachita zoipa ngati Kaini. Koma mmodzi anali wosiyana. Ndiye munthu’yu Enoke. Enoke anali munthu wolimba mtima. Anthu onse om’zungungulira anali kuchita zoipa kwambiri, koma iye anatumikirabe Mulungu.

Kodi mukudziwa chifukwa chake anthu kale’lo anachita zinthu zoipa zambiri? Taganiziranitu, kodi anachititsa Adamu ndi Hava kusamvera Mulungu ndi kudya chipatso choletsedwa ndi Mulungu ndani? Inde, anali mngelo woipa. Baibulo limam’cha Satana. Iye akuyesa kuipitsa ali yense.

Tsiku lina Yehova anauza Enoke kuuza anthu kanthu kena kamene sanafune kukamva. Ndiko: ‘Tsiku lina Mulungu adzaononga anthu onse oipa.’ Anthu’wo anaipidwa kumva izi. Iwo anayesa’di kum’pha. Chotero iye anafunikira kulimba mtima kwambiri kuti auze anthu’wo zodzachitidwa ndi Mulungu.

Mulungu sanalole kuti Enoke akhalitse pakati pa anthu oipa’wo. Iye anakhala ndi moyo zaka 365 zokha. Bwanji tikuti “zaka 365 zokha”? Chifukwa anthu m’nthawi’yo anali amphamvu kwambiri koposa tsopano ndipo anakhala ndi moyo kotalikirapo. Eya, mwana wa Enoke Metusela anakhala ndi moyo zaka 969!

Atafa Enoke, anthu’wo anaipira-ipira. Baibulo limati ‘chiri chonse chimene analingalira chinali choipa nthawi zonse,’ n’kuti ‘dziko lapansi linadzala chiwawa.’

Kodi mukudziwa chifukwa chake panali bvuto lalikulu pa dziko m’masiku’wo? N’chifukwa chakuti Satana anali ndi njira yatsopano yochititsira anthu kuchita zoipa. Tidzaphunzira za izi kenako.

Genesis 5:21-24, 27; 6:5; Ahebri 11:5; Yuda 14, 15.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena