Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 13
  • Abrahamu—Bwenzi la Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Abrahamu—Bwenzi la Mulungu
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Abulahamu ndi Sara Anamvera Mulungu
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
    Nsanja ya Olonda—2001
  • Kodi Abulahamu Anali Ndani?
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Kodi Muli ndi Chikhulupiriro Chonga cha Abrahamu?
    Nsanja ya Olonda—1999
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 13

NKHANI 13

Abrahamu—Bwenzi la Mulungu

AMODZI a malo kumene kunamka anthu chitapita Chigumula anali Uri. Anakhala mzinda wofunika kwambiri wa nyumba zabwino kwambiri. Koma anthu’wo kumene’ko analambira milungu yonyenga. Anachita’nso motero m’Ba’bele. Anthu’wo mu Uri ndi Ba’bele sanali ngati Nowa ndi mwana wake Semu, amene anatumikirabe Yehova.

Zaka 350 pambuyo pa chigumula, Nowa anafa. Panangopita zaka ziwiri zokha pamene munthu mukumuona pa chithunzi’yu anabadwa. Iye anali wapadera kwambiri kwa Mulungu. Dzina lake linali Abrahamu. Iye ndi banja lake anakhala muno mu mzinda wa Uri.

Tsiku lina Yehova anati kwa Abrahamu: ‘Siya Uri ndi abale ako, nupite ku dziko limene ndidzakulozera.’ Kodi anamvera nasiya zokondweretsa zonse za Uri? Inde. Chinali chifukwa cha kumvera Mulungu nthawi zonse uku kuti iye anadziwika kukhala bwenzi la Mulungu.

Ena a m’banja la Abrahamu anatuluka naye mu Uri. Atate wake Tera anamka naye. Mphwake Loti anamka naye. Mkazi wake Sara, anamka naye. Kenako anafika pa malo ochedwa Harana, kumene Tera anafera. Iwo anali kutali kwambiri ndi Uri.

Patapita nthawi iye ndi banja lake anachoka ku Harana nafika ku Kanani. Uko Yehova anati: ‘Iri ndiro dziko limene ndidzapatsa ana ako.’ Abrahamu anakhala m’mahema m’Kananimo.

Mulungu anayamba kuthandiza Abrahamu kwakuti anakhala ndi nkhosa ndi zifuyo zina zochuluka ndi atumiki mazana. Koma iye ndi Sara analibe ana ao ao.

Abrahamu afafika 99, Yehova anati kwa iye: ‘Ndikukulonjeza kuti udzakhala atate wa mitundu yambiri ya anthu.’ Kodi izi zikanachitika motani, pakuti Abrahamu ndi Sara anali okalamba kosati n’kubala mwana?

Genesis 11:27-32; 12:1-7; 17:1-8, 15-17; 18:9-19.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena