Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 50
  • Akazi Awiri Olimba Mtima

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Akazi Awiri Olimba Mtima
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Mtsogoleri Watsopano ndi Azimayi Awiri Olimba Mtima
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • “Ine Ndinauka Monga Mayi mu Isiraeli”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Ndi Chikhulupiriro, Baraki Anagonjetsa Gulu Lankhondo Lamphamvu
    Nsanja ya Olonda—2003
  • Kudzipereka Kwathu Kumachititsa Kuti Yehova Atamandidwe
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 50

NKHANI 50

Akazi Awiri Olimba Mtima

POLOWA m’bvuto Aisrayeli, akupfuulira kwa Yehova. Yehova akuwayankha mwa kuwapatsa atsogoleri olimba mtima kuwathandiza. Baibulo limacha atsogoleri amene’wa Oweruza. Yoswa anali woweruza woyamba, ndipo oweruza ena om’tsatira anali Otiniyeli, Ehudi ndi Samagara. Koma anthu awiri amene anathandiza Israyeli ndiwo akazi Debora ndi Yaeli.

Debora ndiye mneneri wachikazi. Yehova akum’patsa chidziwitso cha za m’tsogolo, ndiyeno iye akuuza anthu zimene Yehova wanena. Debora ali’nso woweruza. Iye akukhala pansi pa mgwalangwa m’dziko la mapiri, ndipo anthu akudza kwa iye kudzathandizidwa zobvuta zao.

Pa nthawi’yi Yabini ndiye mfumu ya Kanani. Iye ali ndi magaleta ankhondo 900. Gulu lake lankhondo n’lamphamvu kwambiri kwakuti Aisrayeli ambiri akakamizika kukhala atumiki a Yabini. Mkulu wa gulu lankhondo la Mfumu Yabini ndiye Sisera.

Tsiku lina Debora akutumiza mthenga kwa Woweruza Baraki, namuuza kuti: ‘Yehova wati: “Tenga amuna 10,000 ndi kumka nawo ku Phiri la Tabori. Kumene’ko ndidzakupatsa Sisera. Ndipo ndidzakupatsani chipambano pa iye ndi ankhondo ake.”’

Baraki akuuza Debora kuti: ‘Ndidzapita ngati mumka nane.’ Debora akumka nawo, koma akuti kwa Baraki: ‘Usadzitamandira pa chipambano’chi, pakuti Yehova adzapereka Sisera m’dzanja la mkazi.’ Ndipo izi ndizo zimene zikuchitika.

Baraki akutsika ku Phiri la Tabori kukakumana ndi ankhondo a Sisera. Mwadzidzidzi Yehova akuchititsa liyambwe, ndipo ankhondo ambiri a mdani akumizidwa. Koma Sisera sakutsika pa gareta wake nathamanga.

Patapita kanthawi Sisera akufika pa hema wa Yaeli. Akum’lowetsa, nam’patsa mkaka. Uwo ukum’gonetsa tulo, ndipo m’kanthawi wagona tulo tatikulu. Ndiyeno Yaeli akutenga chikhomo cha hema n’kuchikhomera m’mutu wa munthu woipa’yu. Pambuyo pake, Baraki akudza, iye akum’sonyeza Sisera wakufa’yo! Chotero mungaone kuti zimene Debora ananena zinakwaniritsidwa.

Potsiriza naye’nso Mfumu Yabini akuphedwa, ndipo Aisrayeli ali ndi mtendere kwa kanthawi.

Oweruza 2:14-22; 4:1-24; 5:1-31.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena