Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gt mutu 22
  • Ophunzira Anayi Aitanidwa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ophunzira Anayi Aitanidwa
  • Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Nkhani Yofanana
  • Yesu Anaitana Ophunzira Ake 4
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Kutumikira Monga Asodzi a Anthu
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Anathetsa Mantha Ndiponso Mtima Wokayikira
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Anathetsa Mantha Ndiponso Mtima Wokayikira
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
Onani Zambiri
Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
gt mutu 22

Mutu 22

Ophunzira Anayi Aitanidwa

PAMBUYO pakuyesayesa kufuna kupha mwambanda moyo wa Yesu m’tauni yakwawo ku Nazarete, iye akusamukira kumzinda wa Kapernao pafupi ndi Nyanja ya Galileya. Zimenezi zikukwaniritsa ulosi wina wa Yesaya. Ndiwo umene unaneneratu kuti anthu a ku Galileya okhala pafupi ndi nyanja adzawona kuunika kwakukulu.

Pamene Yesu akupitiriza ntchito yake yonyamula kuunika ya kulalikira Ufumu kunoko, iye akupeza anayi a ophunzira ake. Ameneŵa anayendapo naye poyambirirapo koma anamka kubizinesi lawo la usodzi pamene anabwerera ndi Yesu kuchokera ku Yudeya. Mwachiwonekere, Yesu akuwafunafuna, popeza kuti ndiyo nthaŵi yabwino ya kukhala ndi othandiza a nthaŵi zonse amene angawaphunzitse kupitiriza uminisitala iye atapita.

Chotero pamene Yesu akuyenda m’mphepete mwa nyanja nawona Simoni Petro ndi atsamwali ake akutsuka makoka awo, akupita kwa iwo. Akukwera bwato la Petro ndi kumuuza kuti akankhe pang’ono bwatolo. Pamene apalasa pang’ono, Yesu akukhala pansi m’bwato ndi kuyamba kuphunzitsa makamu amene ali m’mphepete mwanyanja.

Pambuyo pake, Yesu akunena kwa Petro kuti: “Kankhira kwakuya, nimuponye makoka anu kukasodza.”

“Ambuye,” Petro akuyankha motero, “tinagwiritsa ntchito usiku wonse osakola kanthu, koma pamawu anu ndidzaponya makoka.”

Pamene makoka aponyedwa, nsomba zambiri zedi zikugwidwa kwakuti makoka akuyamba kung’ambika. Mofulumira, amunawo akukodola anzawo a m’bwato lapafupipo kuti abwere kudzawathandiza. Mwamsanga mabwato onse aŵiri adzaza ndi nsomba zambiri kwakuti akuyamba kumira. Powona zimenezi, Petro akugwada pamaso pa Yesu nanena kuti: “Muchoke kwa ine Ambuye, chifukwa ndine munthu wochimwa.”

“Usawope,” Yesu akuyankha motero. “Kuyambira tsopano udzakhala msodzi wa anthu.”

Yesu akuitananso mbale wa Petro Andreya. “Tiyeni pambuyo panga,” akuwafulumiza motero, “Ndidzakusandutsani asodzi a anthu.” Mabwenzi awo osodza nawo Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, akupatsidwa chiitano chimodzimodzicho, ndipo nawonso akulabadira mosazengeleza. Chotero anayi ameneŵa akusiya bizinesi lawo losodza nakhala otsatira oyamba anayi okhazikika, a Yesu. Luka 5:1-11; Mateyu 4:13-22; Marko 1:16-20; Yesaya 9:1, 2.

▪ Kodi nchifukwa ninji Yesu akuitana ophunzira ake kumtsatira, ndipo ameneŵa ndani?

▪ Kodi ndichozizwitsa chotani chimene chikuchititsa mantha Petro?

▪ Kodi ndikusodza kotani kumene Yesu akuitanira ophunzira ake kuchita?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena