Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • sp tsamba 4-6
  • Kodi Anthu Akafa Amapita Kudziko la Mizimu?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Anthu Akafa Amapita Kudziko la Mizimu?
  • Kodi Mizimu ya Akufa Ilipodi?
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Chimachitika N’chiyani Munthu Akamwalira??
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kodi Makolo Athu Ali Kuti?
    Njira ya ku Moyo Wosatha—Kodi Mwaipeza?
  • Chigawo 4
    Mverani Mulungu
  • Kodi Munthu Akafa Amapita Kuti?
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
Onani Zambiri
Kodi Mizimu ya Akufa Ilipodi?
sp tsamba 4-6

Kodi Anthu Akafa Amapita Kudziko la Mizimu?

Anthu ambiri amaganiza kuti munthu akamwalira amapita kumwamba kapena kumidima, koma zimenezi si zoona. Tikutero chifukwa cha zimene Baibulo limanena. Yehova Mulungu ndi amene analenga anthu ndipo amadziwa bwino zimene zimachitika munthu akamwalira.​—Salimo 83:18; 2 Timoteyo 3:16.

Adamu akupangidwa kuchokera ku fumbi

Adamu anapangidwa kuchokera ku fumbi, ndipo atafa anabwereranso ku fumbi

Baibulo limanena kuti Mulungu analenga Adamu “kuchokera kufumbi” n’kumuika m’munda wa Edeni. (Genesis 2:7) Ngati Adamu akanamvera lamulo limene Yehova anamupatsa, sakanafa. Koma sanamvere ndipo Mulungu anati: ‘Udzabwerera kunthaka, pakuti n’kumene unatengedwa. Popeza ndiwe fumbi, kufumbiko udzabwerera.’​—Genesis 3:19.

Kodi Adamu asanalengedwe kuchokera kufumbi, anali kuti? Iye kunalibeko komanso sanali mzimu kumwamba. Choncho pamene Yehova ankamuuza kuti “udzabwerera kunthaka,” ankatanthauza kuti adzafa. Iye atafa sanapite kudziko la mizimu ndipo sanakhalenso ndi moyo kwinakwake.

Kodi anthu ena amene anamwalira, nawonso kulibe? Baibulo limayankha kuti:

  • “Zonse [anthu komanso nyama] zimapita kumalo amodzi. Zonse zinachokera kufumbi ndipo zonse zimabwerera kufumbi.”​—Mlaliki 3:20.

  • “Akufa sadziwa chilichonse.”​—Mlaliki 9:5.

  • “Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo zatha kale.”​—Mlaliki 9:6.

  • “Kulibe kugwira ntchito, kuganiza zochita, kudziwa zinthu, kapena nzeru, ku Manda kumene ukupitako.”​—Mlaliki 9:10.

  • “Iye amabwerera kunthaka. Pa tsiku limenelo zonse zimene anali kuganiza zimatheratu.”​—Salimo 146:4.

Mzimayi akutsuka tomato ndi zinthu zina; azibambo akuluka mabasiketi; azibambo ndi azimayi akumanga nyumba

Amoyo ndi amene angagwire ntchito izi

Kuti mumvetse bwino malembawa, taganizirani izi: M’mabanja ambiri bambo ndi amene amapeza ndalama kuti asamalire banja lake ndipo akamwalira banjalo limavutika kwambiri. Nthawi zina mkazi ndi ana ake amasowa chakudya. Mwinanso amazunzidwa ndi adani a bamboyo. Ndiyeno tingafunse kuti: ‘Ngati bamboyo ali ndi moyo kudziko la mizimu, n’chifukwa chiyani sapitiriza kusamalira banja lake? N’chifukwa chiyani sateteza banja lake kwa adani ake?’ Zonsezi ndi umboni wakuti zimene Baibulo limanena ndi zoona. Bamboyo salinso moyo ndipo sangachite chilichonse.​—Salimo 115:17.

Mzimayi wamasiye ndi ana ake akupempha chakudya; mwana akuona pamene bambo wina akumenya mayi ake

Akufa sangatipatse chakudya kapena kutiteteza

Kodi zimenezi zikutanthauza kuti anthu amene anamwalira sadzakhalanso ndi moyo? Ayi. M’mutu wina kutsogoloku tidzakambirana zoti akufa adzauka. Koma panopa anthu akufa sadziwa chilichonse. Iwo sangathe kutiona, kutimva kapena kutiyankhula. Sitiyenera kuwadalira kapena kuwaopa.​—Mlaliki 9:4; Yesaya 26:14.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena