Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • rq phunziro 1 tsamba 3
  • Mmene Mungadziŵire Zimene Mulungu Amafuna

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mmene Mungadziŵire Zimene Mulungu Amafuna
  • Kodi Mulungu Amafunanji kwa Ife?
  • Nkhani Yofanana
  • Baibulo Ndi Buku Lochokera kwa Mulungu
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Kodi Uthenga Wabwino ndi Wochokeradi kwa Mulungu?
    Uthenga Wabwino Wochokera kwa Mulungu
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kuphunzitsidwa ndi Mulungu?
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Kalata Yochokera kwa Mulungu Amene Amatikonda
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
Onani Zambiri
Kodi Mulungu Amafunanji kwa Ife?
rq phunziro 1 tsamba 3

Phunziro 1

Mmene Mungadziŵire Zimene Mulungu Amafuna

Kodi ndi chidziŵitso chofunika chotani chimene chimapezeka m’Baibulo? (1)

Kodi mlembi wa Baibulo ndani? (2)

N’chifukwa ninji muyenera kuphunzira Baibulo? (3)

1. Baibulo ndi mphatso yamtengo wapatali yochokera kwa Mulungu. Lili ngati kalata imene atate wachikondi walembera ana ake. Limatiuza choonadi ponena za Mulungu—chimene iye ali ndi zimene amafuna. Limatiuza mochitira ndi mavuto ndi mmene tingapezere chimwemwe choona. Baibulo lokhalo limatiuza zimene tiyenera kuchita kuti tikondweretse Mulungu.—Salmo 1:1-3; Yesaya 48:17, 18.

2. Baibulo linalembedwa ndi amuna osiyanasiyana okwanira ngati 40 panyengo ya zaka 1,600, kuyambira mu 1513 B.C.E. Lapangidwa ndi mabuku aang’ono 66. Olemba Baibulo anauziridwa ndi Mulungu. Analemba malingaliro ake, osati awoawo ayi. Chotero Mulungu wakumwamba ndiye Mlembi Wamkulu wa Baibulo, osati munthu aliyense padziko lapansi.—2 Timoteo 3:16, 17; 2 Petro 1:20, 21.

3. Mulungu anatsimikiza kuti Baibulo linakopedwa molondola ndi kusungidwa. Mabaibulo ambiri asindikizidwa kuposa buku lina lililonse. Si onse amene adzakondwa kukuonani mukuphunzira Baibulo, koma musalole zimenezo kukuletsani. Mtsogolo mwanu mosatha mumadalira pa kudziŵa kwanu Mulungu ndi kuchita chifuniro chake mosasamala kanthu za chitsutso chilichonse.—Mateyu 5:10-12; Yohane 17:3.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena