Mayiko Otchulidwa M’baibulo
AISRAYELI ali m’kati mokonzekera kuloŵa m’Dziko Lolonjezedwa, Mose anapempha Mulungu chimene mtima wake unali kulakalaka. Iye anati: “Ndiwoloketu, ndilione dziko lokomali lili tsidya la Yordano, mapiri okoma aja.”—Deut. 3:25.
Chimene Mose anapemphacho sichinatheke, koma anakwera m’phiri lina loyang’anizana ndi Yeriko n’kuliona dzikolo. Anaona, ‘Gileadi, kufikira ku Dani ndi dziko la Yuda kufikira nyanja ya m’tsogolo ndi [ku Negebu], ndi chigwa cha Yordano.’ (Deut. 3:27; 34:1-4) Kodi munamvapo mayina ameneŵa? Kodi mukudziŵa kumene anali?
Mwa anthu a Yehova lerolino ndi anthu oŵerengeka chabe amene angathe kupita kukaona malo ambiri amene nkhani zake amaziŵerenga m’Baibulo. Satha kuchita zomwe Mulungu anauza Abrahamu kuti achite, zoyendayenda m’litali ndi m’mimba mwa Dziko Lolonjezedwa. (Gen. 13:14-17) Komabe Akristu oona ali ndi chidwi chofuna kudziŵa za malo otchulidwa m’Baibulo ndiponso kuona mmene malowo akugwirizanirana ndi malo ena.
‘Onani Dziko Lokoma’ ndi buku limene mungaligwiritse ntchito kuti muwamvetse bwino Malemba. Lili ndi zithunzi zosonyeza mmene madera ena alili panopo, monga dera la Gileadi lomwe talisonyeza pachikuto. Mungaphunzire zambiri kudzera m’mapu a m’buku lino, omwe angakuthandizeni kudziŵa bwino malo otchulidwa m’Baibulo.
Mapu omwe ali pamasamba 2 ndi 3 akusonyeza makamaka mayiko kapena madera akuluakulu. Mwachitsanzo, mutaona pamene Asuri ndi Igupto anali poyerekeza ndi Dziko Lolonjezedwa, mungamvetse maulosi amene amanena za mayiko ameneŵa. (Yes. 7:18; 27:13; Hos. 11:11; Mika 7:12) Chigawo chaching’ono chotchedwa kuti Dziko Lolonjezedwa chinali dera lomwe kalelo munkadutsa njira zambiri, ndipo mitundu ina inkafuna kumalamulira nthaka yake yachonde yolola mbewu zosiyanasiyana, minda yamphesa, ndiponso mitengo ya azitona.—Deut. 8:8; Ower. 15:5.
Nthaŵi zina mungafunike kuyerekeza mapu angapo. Mwachitsanzo, Yona anatumidwa ku likulu la Asuri, koma iye anakwera chombo kupita ku Tarisi. (Yona 1:1-3) Kodi madera ameneŵa akupezeka pamapu oyamba aja? Komatu osasokoneza Tarisi ndi Tariso, komwe mtumwi Paulo anabadwira. Pamapu ali panoŵa mungapezepo Tariso ndiponso mizinda ina yotchuka.
Taganizirani za mtunda ndiponso njira yomwe Abrahamu anadutsa paulendo wake mutapeza pamene pali Uri, Harana, ndi Yerusalemu. Yehova atauza Abrahamu kuti achoke ku Uri, iye anakakhala ku Harana ndipo kenako anasamukira ku Dziko Lolonjezedwa. (Gen. 11:28–12:1; Mac. 7:2-5) Muumvetsa bwino ulendo wa Abrahamu mukaŵerenga nkhani yakuti “Moyo wa Makolo Akale,” pamasamba 6 mpaka 7.
Mapu oyamba aja ndiponso aŵa ali panoŵa sakunena za nthaŵi iliyonse. Koma mapu ena onse akuyenderana ndithu ndi zochitika zofotokozedwazo. Midzi kapena zina ndi zina zosonyezedwa pamapupo, zikukhudza zinthu zimene zinachitika panthaŵi ina yake. Ngakhale kuti Mlozera Malo (pamasamba 34-35) alibe malo onse omwe asonyezedwa m’mapu, angakuthandizenibe kudziŵa kuti ndi mapu ati amene akufotokoza za mfundo yomwe mukufufuzayo.
Mapu omwe ali pakati (pamasamba 18-19) ali ndi midzi yambiri ya m’Dziko Lolonjezedwa. Bokosi la Zizindikiro za Pamapu lingakuthandizeni kupeza midzi ya Alevi ndiponso midzi isanu ndi umodzi yopulumukirako komanso lingakuthandizeni kudziŵa ngati malo ena ake anatchulidwa m’Malemba Achihebri, m’Malemba Achigiriki, kapena m’Malemba Achihebri ndi Achigiriki omwe.
Pakalipano malo ena otchulidwa m’Baibulo sakudziŵika kuti anali pati, motero mapu amene ali pakatiwo alibe malo ambiri oterowo. Komanso, sizinatheke kusonyeza midzi yonse yomwe ili pa mndandanda wa malire a mafuko. (Yos., machaputala 15-19) Komabe mapu ameneŵa ali ndi midzi yoyandikana nayo, motero mungathe kungoyerekezera pamene panali midziyo. Taika zizindikiro pa zinthu zina zachilengedwe (monga mapiri, mitsinje, ndiponso zigwa), ndipo kukwera komanso mmene malowo alili tazisonyeza ndi mitundu yosiyanasiyana. Zimenezi zingakuthandizeni kukhala ngati mukuona zochitika zofotokozedwa m’Baibulo.
Buku la Insight on the Scriptures, limafotokoza zambiri zokhudza malo otchulidwa m’Baibulo, ndipo bukuli limapezeka m’zinenero zambiri.a Pamene mukugwiritsa ntchito buku limenelo ndi mabuku ena othandiza pophunzira Baibulo, buku lino lakuti ‘Onani Dziko Lokoma’ lizikhala pafupi. Ligwiritseni ntchito pamene mukuphunzira Malemba onse amene ali opindulitsa kwambiri pamoyo wanu.—2 Tim. 3:16, 17.
[Mawu a M’munsi]
a Lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova.
[Bokosi patsamba 5]
MABUKU A BAIBULO ANALEMBEDWERA KU
Babulo
Kaisareya
Korinto
Igupto
Efeso
Yerusalemu
Makedoniya
Moabu
Patmo
Dziko Lolonjezedwa
Roma
Susani
[Mapu patsamba 4, 5]
(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)
Bible Lands and Key Cities
A1 ITALIYA
A2 ROMA
A3 SICILY
A3 MALTA
C2 MAKEDONIYA
C2 Filipi
C2 GIRISI
C3 ATENE
C3 Korinto
C3 KRETE
C4 LIBYA
D3 Antiokeya (ku Pisidiya)
D3 Efeso
D3 PATMO
D3 RODE
D4 MOFI
D5 IGUPTO
E2 ASIYA MINA
E3 Tariso
E3 Antiokeya (ku Suriya)
E3 KUPRO
E4 Sidoni
E4 Damasiko
E4 Turo
E4 Kaisareya
E4 DZIKO LOLONJEZEDWA
E4 YERUSALEMU
E4 MOABU
E4 Kadesi
E4 EDOMU
F3 Munda wa Edene?
F3 ASURI
F3 Harana
F3 SURIYA
F5 ARABIYA
G3 NINEVE
G4 BABULO
G4 KALDAYO
G4 Susani
G4 Uri
H3 MEDIYA
[Mapiri]
E5 Phiri la Sinai
G2 MAPIRI A ARARATI
[Nyanja]
C3 Nyanja ya Mediterranean (Nyanja Yaikulu)
E1 Nyanja Yakuda
E5 Nyanja Yofiira
H2 Nyanja ya Caspian
H5 Nyanja ya Perisiya
[Mitsinje]
D5 Mtsinje wa Nile
F3 Mtsinje wa Firate
G3 Mtsinje wa Tigirisi