Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gl tsamba 6-7
  • Moyo wa Makolo Akale

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Moyo wa Makolo Akale
  • ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Nkhani Yofanana
  • B2 Chiyambi Komanso Maulendo a Atumiki Akale
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Maufumu Athira Nkhondo Dziko Lolonjezedwa
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
    Nsanja ya Olonda—2001
  • Yehova Ndi “Mulungu Amene Amapatsa Mtendere”
    Nsanja ya Olonda—2011
Onani Zambiri
‘Onani Dziko Lokoma’
gl tsamba 6-7

Moyo wa Makolo Akale

STEFANO anayamba nkhani yake yotchuka mwa kutchula malo osiyanasiyana. Iye anati: “[Yehova] anaonekera kwa kholo lathu Abrahamu, pokhala iye m’Mesopotamiya, asanayambe kukhala m’Harana; nati kwa iye, Tuluka . . . tiye ku dziko limene ndidzakusonyeza iwe.” (Mac. 7:1-4) Pamenepa m’pamene panayambira zochitika zosiyanasiyana zofunika kwambiri m’Dziko Lolonjezedwa zokhudza Abrahamu, Isake, ndi Yakobo. Zochitika zimenezo zinali zogwirizana ndi cholinga cha Mulungu chakuti adalitse anthu onse.—Gen. 12:1-3; Yos. 24:3.

Mulungu anauza Abrahamu (kapena kuti, Abramu) kuti achoke ku Uri wa Akaldayo, mudzi wotukuka umene kalelo unali kum’maŵa kwa Mtsinje wa Firate m’mphepete mwake. Kodi Abrahamu akanadutsa njira iti? Kuchokera ku Kaldayo, dera lotchedwanso Sumer kapena Sinara, kukanakhala kosavuta kungopita kumadzulo mwachindunji. Nanga anazungulira bwanji kudzera ku Harana kutaliko?

Mmene Makolo Akale Anayendera M’Dziko Lolonjezedwa

Uri anali kum’maŵa chakumapeto kwa dera lina lachonde lotchedwa Fertile Crescent, lomwe linayambira ku Palestina mpaka ku chigwa cha mitsinje ya Tigirisi ndi Firate. N’kutheka kuti kalelo dera limeneli linali losatentha ndiponso losazizira kwambiri. M’munsi mwa derali munali Chipululu cha Suriya ndi Arabiya chimene chinali ndi mapiri a miyala ya njereza ndi madera a mchenga. Buku la The Encyclopædia Britannica limanena kuti dera limeneli linali “lovuta kwambiri kudutsamo pamaulendo apakati pa Gombe la Mediterranean ndi Mesopotamiya.” Apaulendo ayenera kuti anali kudutsa deralo kuchokera ku Firate kupita ku Tadimori kenako n’kulunjika ku Damasiko, koma Abrahamu sanadutsitse banja lake ndi zoŵeta zake m’chipululu chimenecho.

M’malo mwake, Abrahamu anatsata chigwa cha Mtsinje wa Firate mpaka ku Harana. Kuchokera kumeneko anadutsa njira imene amalonda anali kudutsa mpaka atafika pamalo owolokera ku Karikemesi. Kenako analunjika kum’mwera kudutsa ku Damasiko mpaka anafika kunyanja imene inadzatchedwa Nyanja ya Galileya. Njira yotchedwa Via Maris, kapena kuti “Njira Yodutsa Kunyanja,” inadzera ku Megido mpaka ku Igupto. Koma Abrahamu anadutsa kumapiri a Samariya, ndipo anakhala m’mahema ku Sekemu. Patapita nthaŵi, anapitiriza ulendo wake wa kum’mwera kudutsa njira ya kumapiri imeneyo. M’tsatireni pamene mukuŵerenga Genesis 12:8–13:4. Onani malo ena amene iye anadutsako pamoyo wake: Dani, Damasiko, Hoba, Mamre, Sodomu, Gerari, Beereseba, ndi Moriya (Yerusalemu).—Gen. 14:14-16; 18:1-16; 20:1-18; 21:25-34; 22:1-19.

Kudziŵa za malowo kumathandiza kumvetsa zimene zinachitika pamoyo wa Isake ndi Yakobo. Mwachitsanzo, mmene Abrahamu anali ku Beereseba, kodi n’kuti kumene anatuma wantchito wake kuti akapezere Isake mkazi? Anam’tuma kutali ku Mesopotamiya (kutanthauza, “Dziko la Pakati pa Mitsinje”) ku Padanaramu. Ndiye taganizirani za ulendo wovuta umene Rebeka anayenda pa ngamila kupita ku Negebu, mwina pafupi ndi Kadesi, kukakumana ndi Isake.—Gen. 24:10, 62-64.

Panthaŵi ina m’tsogolo Yakobo (Israyeli) mwana wawo, anayenda ulendo wofananawo kuti akakwatire mkazi wolambira Yehova. Koma pobwerera kwawo, Yakobo anadutsa njira ina. Atawoloka Yaboki pafupi ndi Penieli, Yakobo analimbana ndi mngelo. (Gen. 31:21-25; 32:2, 22-30) Esau anakumana naye m’dera limenelo, ndipo Yakobo ndi Esau anakakhala kumadera osiyana.—Gen. 33:1, 15-20.

Makolo Akale M’Dziko Lolonjezedwa

Dina mwana wa Yakobo atagwiriridwa ku Sekemu, Yakobo anasamuka kukakhala ku Beteli. Koma kodi mungayerekezere mtunda umene ana a Yakobo anafikako podyetsa nkhosa zake, kumene Yosefe anakawapeza? Mapu ali pano (ndi pamasamba 18-19) angakuthandizeni kuona mtunda umene unali pakati pa Beteli ndi Dotana. (Gen. 35:1-8; 37:12-17) Abale a Yosefe anam’gulitsa kwa amalonda amene anali kupita ku Igupto. Kodi mukuganiza kuti amalondawo, pa chochitika chimene chinachititsa kuti Aisrayeli asamukire ku Igupto ndi kudzachokako, anadutsa njira iti?—Gen. 37:25-28.

[Mapu patsamba 7]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Maulendo a Abrahamu (Onani m’kabuku kenikeni)

Maulendo a Isake (Onani m’kabuku kenikeni)

Maulendo a Yakobo (Onani m’kabuku kenikeni)

Njira Zazikulu (Onani m’kabuku kenikeni)

Maulendo a Makolo Akale

A4 GOSHENI

A5 IGUPTO

B4 SURI

B5 PARANA

C3 Damasiko

C3 Dani (Laisi)

C4 Sekemu

C4 Beteli

C4 Hebroni (Kiriyati-araba)

C4 Gerari

C4 Beereseba

C4 SEIRI

C4 Kadesi

C5 EDOMU

D1 Karikemesi

D2 Tadimori

D3 Hoba

E1 PADANARAMU

E1 Harana

F2 MESOPOTAMIYA

G1 Nineve

G2 FERTILE CRESCENT

G3 Babulo

H4 KALDAYO

H4 Uri

[Mapiri]

C4 Moriya

[Nyanja]

B3 Nyanja ya Mediterranean (Nyanja Yaikulu)

[Mitsinje]

E2 Firate

G2 Tigirisi

Makolo Akale (m’Dziko Lolonjezedwa)

KANANI

Megido

GILEADI

Dotana

Sekemu

Sukoti

Mahanaimu

Penieli

Beteli (Luzi)

Ai

Yerusalemu (Salemu)

Betelehemu (Efrati)

Mamre

Hebroni (Makipela)

Gerari

Beereseba

Sodomu?

NEGEBU

Rehoboti?

Beerelahai-roi

Kadesi

[Njira Zazikulu]

Via Maris

Msewu Wachifumu

[Mapiri]

Moriya

[Nyanja]

Nyanja ya Mchere

[Mitsinje]

Yaboki

Yordano

[Chithunzi patsamba 6]

Mtsinje wa Firate pafupi ndi Babulo

[Chithunzi patsamba 6]

Abrahamu anakhala ku Beereseba ndipo ankadyetsa nkhosa zake chapafupi

[Chithunzi patsamba 6]

Chigwa cha Yaboki

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena