Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gl tsamba 30-31
  • Yerusalemu ndi Kachisi Amene Yesu Ankamudziŵa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yerusalemu ndi Kachisi Amene Yesu Ankamudziŵa
  • ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Nkhani Yofanana
  • B11 Kachisi Wapaphiri mu Nthawi ya Yesu
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
    Nsanja ya Olonda—2002
  • Yerusalemu ndi Kachisi wa Solomo
    ‘Onani Dziko Lokoma’
‘Onani Dziko Lokoma’
gl tsamba 30-31

Yerusalemu ndi Kachisi Amene Yesu Ankamudziŵa

Yerusalemu/Kachisi wa Herode

PATAPITA nthaŵi pang’ono Yesu atabadwa, Yosefe ndi Mariya anamutenga kupita naye kumzinda wa Yerusalemu kumene Atate wake wakumwamba anaikako dzina Lake. (Luka 2:22-39) Ali ndi zaka 12, Yesu anapitanso ku Yerusalemu ku Paskha. Iye anadabwitsa aphunzitsi a pakachisi ndi nzeru zake. (Luka 2:41-51) Ntchito yomanga kachisiyo, yomwe inali ina mwa ntchito zambiri zomanga za Herode Wamkulu, inatenga “zaka makumi anayi ndi zisanu ndi chimodzi.”—Yoh. 2:20.

Pa utumiki wake, Yesu anali kukhala nawo pa maphwando ku Yerusalemu, kumene nthaŵi zambiri anali kuphunzitsa anthu ambirimbiri. Kaŵiri konse anathamangitsa anthu osintha ndalama ndi amalonda kuwachotsa m’bwalo la kachisi.—Mat. 21:12; Yoh. 2:13-16.

Kumpoto kwa kachisiyo, pathamanda la Betesda, Yesu anachiritsa munthu yemwe anadwala zaka 38. Mwana wa Mulungu ameneyu anachiritsanso munthu wakhungu, yemwe anamuuza kuti akasambe m’thamanda la Siloamu lomwe linali kum’mwera kwa mzindawo.—Yoh. 5:1-15; 9:1, 7, 11.

Yesu nthaŵi zambiri anali kukacheza kwa mabwenzi ake Lazaro, Mariya, ndi Marita ku Betaniya, “pafupifupi makilomita atatu” kum’maŵa kwa Yerusalemu. (Yoh. 11:1, 18, NW, mawu a m’munsi; 12:1-11; Luka 10:38-42; 19:29; onani “Dera la Yerusalemu,” patsamba 18.) Patatsala masiku ochepa kuti aphedwe, Yesu anafika ku Yerusalemu podutsira ku Phiri la Azitona. Tangoyerekezerani kuti mukumuona akuima ndi kuyang’ana kumadzulo pa mzindawo, n’kumaulirira. (Luka 19:37-44) Zimene iye anaona zingakhale zofanana ndi zimene mukuona patsamba lotsatirali pamwamba. Kenako Yesu analoŵa m’Yerusalemu atakwera pabulu, ndipo ayenera kuti analoŵera pa chimodzi mwa zipata za kum’maŵa kwa mzindawo. Makamu a anthu anam’tamanda monga Mfumu ya Israyeli ya m’tsogolo.—Mat. 21:9-12.

Zinthu zofunika zimene zinachitika Yesu asanafe, zinachitikira m’Yerusalemu kapena malo ena pafupi ndi mzindawo: m’munda wa Getsemane, kumene Yesu anapemphera; Bwalo la Akulu (Sanihedrini); m’nyumba ya Kayafa; m’nyumba ya Kazembe Pilato ndipo pomaliza ku Gologota.—Marko 14:32, 14:53–15:1, 16, 22; Yoh. 18:1, 13, 24, 28.

Yesu ataukitsidwa, anaonekera ku Yerusalemu ndi malo ena apafupi ndi mzindawu. (Luka 24:1-49) Kenako anakwera kumwamba kuchokera pa Phiri la Azitona.—Mac. 1:6-12.

[Chithunzi patsamba 31]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Jerusalem/Herod’s Temple

Mbali za Kachisi

1. Malo Opatulikitsa

2. Malo Opatulika

3. Guwa la Nsembe Yopsereza

4. Thawale Lamkuwa

5. Bwalo la Ansembe

6. Bwalo la Israyeli

7. Bwalo la Akazi

8. Bwalo la Akunja

9. Mpanda (Soreg)

10. Khumbi Lachifumu

11. Khumbi la Solomo

KACHISI

Chipata

Bwalo la Ansembe

Chipata

Malo Opatulikitsa Guwa la

Malo Opatulika Nsembe Bwalo la Bwalo la

Yopsereza Israyeli Akazi

Thawale

Lamkuwa

Chipata Khumni la

Mpanda (Soreg) Solomo

Bwalo la Akunja

Chipata

Khumbi Lachifumu

Zipata

Nsanja ya Antonia

Mlatho

Bwalo la Akulu? (Sanihedirini)

CHIGWA CHA TYROPOEON

Thamanda la Siloamu

Ngalande

Nyumba ya Kayafa?

Nyumba ya Kazembe

Gologota?

Gologota?

Thamanda la Betesda

Munda wa Getsemane?

PHIRI LA AZITONA

CHIGWA CHA KIDRONI

Kasupe wa Gihoni

Eni-rogeli

CHIGWA CHA HINOMU (GEHENA)

[Zithunzi patsamba 30]

Kuyang’ana kum’maŵa kudutsa Yerusalemu wamakono: (A) malo a kachisi, (B) munda wa Getsemane, (C) Phiri la Azitona, (D) chipululu cha Yudeya, (E) Nyanja Yakufa

[Chithunzi patsamba 31]

Kuyang’ana kumadzulo muli pa Phiri la Azitona m’nthaŵi ya Yesu

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena