Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yp2 tsamba 227
  • Chitsanzo Chabwino—Paulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chitsanzo Chabwino—Paulo
  • Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
  • Nkhani Yofanana
  • Mafunso Ochokera Kwa Owerenga
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
    Nsanja ya Olonda—1991
  • Kodi N’zoona Kuti Yesu Anandifera Ineyo?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Aroma Amva Mbiri Yabwino Koposa
    Nsanja ya Olonda​—1990
Onani Zambiri
Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
yp2 tsamba 227

Chitsanzo Chabwino​—Paulo

Mtumwi Paulo ankadziwa zinthu zimene angathe kuchita komanso zimene sangathe. Iye anati: “Pamene ndikufuna kuchita chinthu chabwino, choipa chimakhala chili nane.” Paulo anali ndi mtima wofuna kuchita zinthu zabwino n’chifukwa chake ananena kuti: “Mu mtima mwanga ndimasangalala kwambiri ndi chilamulo cha Mulungu.” Koma kodi vuto lake linali chiyani? Iye ananena kuti: “Ndimaona chilamulo china . . . chikumenyana ndi chilamulo cha m’maganizo mwanga ndi kundipanga kapolo wa chilamulo cha uchimo chimene chili m’ziwalo zanga.” Paulo sankasangalala chifukwa panali zinthu zina zimene ankalakwitsa. Iye anadandaula kuti: “Munthu wovutika ine!”—Aroma 7:21-24.

Kodi mukalakwitsa zinthu, mumaona kuti ndinu munthu wolephera? Umu ndi mmenenso Paulo ankamvera nthawi zina. Koma Paulo ankadziwanso kuti Khristu anafera anthu ngati iyeyo. Choncho iye ananena kuti: ‘Mulungu adzandipulumutsa kudzera mwa Yesu Khristu Ambuye wathu.’ (Aroma 7:25) Paulo ankaona kuti Yesu anamufera iyeyo payekha. Iye anati: “Mwana wa Mulungu . . . anandikonda nadzipereka yekha chifukwa cha ine.” (Agalatiya 2:20) Mukakhumudwa, muziganizira dipo la Yesu. Ndipo mukalakwitsa zinthu zinazake, muzikumbukira kuti Khristu anafera anthu ochimwa, osati anthu angwiro.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena