Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 22 tsamba 56-tsamba 57 ndime 3
  • Pa Nyanja Yofiira Panachitika Zodabwitsa Kwambiri

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pa Nyanja Yofiira Panachitika Zodabwitsa Kwambiri
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Kuoloka Nyanja Yofiira
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • ‘Yehova Wakhala Chipulumutso Changa’
    Nsanja ya Olonda—2006
  • “Chirimikani, Ndipo Penyani Chipulumutso cha Yehova”
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Mulungu Anapulumutsa Ana a Isiraeli
    Kodi Baibulo Lili Ndi Uthenga Wotani?
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 22 tsamba 56-tsamba 57 ndime 3
Farao ndi asilikali ake

MUTU 22

Zodabwitsa Zimene Zinachitika pa Nyanja Yofiira

Farao atamva kuti Aisiraeli achoka ku Iguputo, anasintha maganizo. Anauza asilikali ake kuti: ‘Tengani magaleta anga ankhondo, tiwatsatire. Sitimayenera kuwalola kuti apite.’ Choncho Farao ndi asilikali ake anayamba kuthamangira Aisiraeli.

Yehova ankatsogolera anthu ake. Masana ankagwiritsira ntchito mtambo ndipo usiku ankagwiritsa ntchito moto. Aisiraeliwo atafika pa Nyanja Yofiira, Yehova anawauza kuti amange misasa.

Kenako Aisiraeli anaona Farao ndi asilikali ake akuwathamangira. Analibe kothawira chifukwa kutsogolo kwawo kunali nyanja ndipo kumbuyo kwawo n’kumene kunali asilikaliwo. Iwo anachita mantha kwambiri ndipo analirira Mose kuti: ‘Tifa basi! Bola ukanangotisiya ku Iguputo konkuja.’ Koma Mose anawauza kuti: ‘Musachite mantha. Limbani mtima ndipo muona mmene Yehova atipulumutsire.’ Apa Mose anasonyeza kuti ankakhulupirira kwambiri Yehova.

Ndiyeno Yehova anauza Aisiraeli kuti anyamuke. Usiku umenewo, Yehova anachititsa kuti mtambo uja ukhale pakati pa Aisiraeliwo ndi Aiguputo. Zimenezi zinachititsa kuti kumbali ya Aiguputo kukhale mdima, pamene kumbali ya Aisiraeli kunkawala.

Yehova anauza Mose kuti atambasule dzanja lake n’kuloza panyanja. Ndiyeno Yehova anachititsa mphepo yamphamvu kuwomba panyanjapo usiku wonse. Kenako nyanjayo inagawikana ndipo madzi anaima ngati makoma m’mbali zonse. Aisiraeli anawoloka pouma kupita kutsidya la nyanjayo.

Aisiraeli akuwoloka pouma, madzi ataima ngati makoma m’mbali zonse

Asilikali a Farao analowa pakati pa makoma amadziwo potsatira Aisiraeli. Zitatero Yehova anachititsa kuti asilikaliwo asokonezeke. Mateyala a magaleta awo anayamba kuguluka. Ataona zimenezi asilikaliwo anafuula kuti: ‘Tiyeni tithawe! Yehova akuwamenyera nkhondo.’

Kenako Yehova anauza Mose kuti: ‘Tambasula dzanja lako ndi kuloza panyanja.’ Nthawi yomweyo madzi aja anabwerera m’malo mwake n’kumiza asilikali onse a Aiguputo. Farao ndi asilikali ake anafera pomwepo. Palibe ngakhale mmodzi amene anapulumuka.

Aisiraeliwo ataona kuti apulumuka anatamanda Mulungu poimba kuti: “Ndiimbira Yehova, chifukwa walemekezeka kwambiri. Mahatchi ndi okwera pamahatchiwo wawaponyera mʼnyanja.” Poimba nyimboyi, azimayi ankavina ndipo ena ankaimba maseche. Aliyense anasangalala kwambiri chifukwa tsopano sanalinso akapolo.

“Tikhale olimba mtima ndithu ndipo tinene kuti: ‘Yehova ndi amene amandithandiza. Sindidzaopa. Munthu angandichite chiyani?’”​—Aheberi 13:6

Mafunso: Kodi n’chiyani chinachitika pa Nyanja Yofiira? Kodi Yehova anapulumutsa bwanji Aisiraeli?

Ekisodo 13:21, 22; 14:1-31; 15:1-21; Nehemiya 9:9-11; Salimo 106:9-12; 136:11-15; Aheberi 11:29

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena