Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 35 tsamba 86-tsamba 87 ndime 1
  • Hana Anapempha Kuti Mulungu Amupatse Mwana Wamwamuna

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Hana Anapempha Kuti Mulungu Amupatse Mwana Wamwamuna
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Anapemphera Kuchokera Pansi pa Mtima
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
  • Anauza Mulungu Zakukhosi Kwake
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Mmene Hana Anapezera Mtendere
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Muzilola Kuti Yehova Azikutonthozani
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2020
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 35 tsamba 86-tsamba 87 ndime 1
Hana akupereka Samueli kwa Eli kuti azitumikira pachihema

MUTU 35

Hana Anapempha Mwana Wamwamuna

Bambo wina wa ku Isiraeli dzina lake Elikana anali ndi akazi awiri. Mayina a akaziwo anali Hana ndi Penina. Koma Elikana ankakonda kwambiri Hana. Penina anali ndi ana ambiri koma Hana analibe ngakhale mmodzi. Chifukwa cha zimenezi, Penina ankanyoza Hana nthawi zonse. Chaka chilichonse, Elikana ankapita kukalambira Mulungu ku Silo limodzi ndi banja lake. Tsiku lina ali kumeneko, anazindikira kuti mkazi wake Hana, amene ankamukonda kambiri, wakhumudwa kwambiri. Iye anamuuza kuti: ‘Hana usalire. Ndimakukonda kwambiri. Kodi si ine woposa ana amene ukufunawo?’

Kenako Hana ananyamuka kupita kukapemphera. Iye anapempha Yehova kuti amuthandize ndipo ankapemphera uku akulira. Hana analonjeza kuti: ‘Yehova, mukandipatsa mwana wamwamuna ndidzakupatsani kuti azikutumikirani kwa moyo wake wonse.’

Eli yemwe anali Mkulu wa Ansembe akuona Hana akupemphera uku akulira

Mkulu wa ansembe dzina lake Eli ataona milomo ya Hana ikugwedera, anaganiza kuti waledzera. Koma Hana anayankha kuti: ‘Ayi, mbuyanga, inetu sindinaledzere. Ndili ndi vuto lalikulu kwambiri limene ndikufotokozera Yehova.’ Eli anazindikira kuti walakwitsa ndipo anauza Hanayo kuti: ‘Mulungu akupatse zimene ukufunazo.’ Zitatero Hana anayamba kumva bwino mumtima ndipo anabwerera. Chaka chisanathe, anabereka mwana n’kumupatsa dzina loti Samueli. Iye ayenera kuti anasangalala kwambiri.

Hana sanaiwale zimene analonjeza kwa Yehova. Samueli atangosiya kuyamwa, anamupereka kuti azikatumikira kuchihema. Iye anauza Eli kuti: ‘Mwana uyu ndi amene ndinkapempha nthawi ijayi. Ndamupereka kuti atumikire Yehova kwa moyo wake wonse.’ Chaka chilichonse, Elikana ndi Hana ankapita kukaona Samueli ndipo ankamutengera malaya atsopano odula manja. Yehova anapatsa Hana ana ena, aamuna atatu ndi aakazi awiri.

“Pitirizani kupempha ndipo adzakupatsani. Pitirizani kufunafuna ndipo mudzapeza.”​—Mateyu 7:7

Mafunso: N’chifukwa chiyani Hana anakhumudwa kwambiri? Kodi Yehova anadalitsa bwanji Hana?

1 Samueli 1:1-28; 2:1-11, 18-21

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena