Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 41 tsamba 100-tsamba 101 ndime 2
  • Davide ndi Sauli

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Davide ndi Sauli
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Chifukwa chake Davide Akuthawa
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Davide Akulongedwa Ufumu
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • “Kumvera Kuposa Nsembe”
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Zimene Zili Mʼbuku la 1 Samueli
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 41 tsamba 100-tsamba 101 ndime 2
Davide akufuula polankhula ndi anthu amene ali ndi Sauli

MUTU 41

Davide ndi Sauli

Davide atangopha Goliyati, Mfumu Sauli inamusankha kuti akhale mkulu wa asilikali. Davide anapambana nkhondo zambiri ndipo anatchuka kwambiri. Akamabwera kunkhondo, akazi ankavina komanso kuimba kuti: ‘Sauli wapha adani masauzande koma Davide wapha masauzande ambirimbiri.’ Sauli anapsa mtima kwambiri moti anayamba kufuna kupha Davide.

Davide ankadziwa kuimba zeze. Tsiku lina akuimbira Sauli nyimbo, Sauliyo anaponya mkondo wake kuti amuphe. Davide anazinda ndipo mkondowo unafikira pakhoma. Kungoyambira pamenepo, Sauli ankayesetsa kuti aphe Davide. Kenako Davide anathawira kuchipululu.

Davide akutenga mkondo wa Sauli pamene Sauliyo ali mtulo

Sauli anatenga asilikali 3,000 n’kumakasakasaka Davide. Ndiyeno tsiku lina analowa kuphanga limene kunali Davide ndi anzake. Anzake a Davidewo anati: ‘Uwutu ndi mwayi wako kuti uphe Sauli.’ Davide anangoyenda chokwawa n’kukadula kansalu pa chovala cha Sauli koma Sauliyo sanadziwe chilichonse. Zitatero, Davide anadandaula kwambiri kuti sanalemekeze mfumu yodzozedwa ndi Mulungu. Iye sanalole kuti anzakewo aphe Sauli. Kenako Sauli atatuluka m’phangamo, Davide anafuula n’kumuuza kuti anali ndi mwayi woti amuphe koma anangomusiya. Kodi Sauli anasintha maganizo?

Ayi ndithu. Anapitirizabe kusakasaka Davide. Tsiku lina usiku, Davide ndi m’bale wake dzina lake Abisai anapita pamalo amene Sauli anagona ndi asilikali ake. Anapeza kuti Abineri, amene anali msilikali wolondera mfumu, nayenso anali atagona. Ndiyeno Abisai anati: ‘Mwayitu suposa apa. Bwanji ndimuphe?’ Koma Davide anati: ‘Ayi, ameneyutu adzalangidwa ndi Yehova. Tiye tingotenga mkondo wake ndi jagi yakeyo tizipita.’

Kenako Davide anakakwera paphiri lina lapafupi n’kufuula kuti: ‘Iwe Abineri! Ukungogona osateteza mfumuyo? Kodi mkondo wa Sauli ndi madzi ake zili kuti?’ Sauli atazindikira mawu a Davide anati: ‘Mpata woti undiphe unaupeza koma wandikomera mtima. Ndazindikira tsopano kuti iwe udzakhaladi mfumu ya Isiraeli.’ Apa tsopano Sauli anabwerera kunyumba kwake. Koma sikuti anthu onse a m’banja la Sauli ankadana ndi Davide.

“Ngati nʼkotheka, yesetsani mmene mungathere kuti muzikhala mwamtendere ndi anthu onse. Okondedwa, musamabwezere zoipa, koma siyirani malo mkwiyo wa Mulungu.”​—Aroma 12:18, 19

Mafunso: N’chifukwa chiyani Sauli ankafuna kupha Davide? N’chifukwa chiyani Davide sanafune kupha Sauli?

1 Samueli 16:14-23; 18:5-16; 19:9-12; 23:19-29; 24:1-15; 26:1-25

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena