Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 43 tsamba 104
  • Tchimo la Mfumu Davide

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tchimo la Mfumu Davide
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Bvuto m’Banja la Davide
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Dalirani Mzimu wa Mulungu Zinthu Zikasintha pa Moyo Wanu
    Nsanja ya Olonda—2004
  • Kulapa Komwe Kumachiritsa
    Nsanja ya Olonda—2001
  • Amakhululukira Munthu wa “Mtima Wosweka ndi Wolapa”
    Nsanja ya Olonda—2010
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 43 tsamba 104
Mneneri Natani akudzudzula Mfumu Davide

MUTU 43

Tchimo la Mfumu Davide

Sauli atafa, Davide anakhala mfumu. Iye anayamba kulamulira ali ndi zaka 30. Tsiku lina ali padenga la nyumba yake anaona mkazi wokongola. Atafufuza anapeza kuti dzina lake anali Bati-seba ndipo anali mkazi wa Uriya,yemwe anali msilikali. Davide anaitanitsa mkaziyo kuti abwere kunyumba kwake. Iye anagona naye ndipo mkaziyo anakhala oyembekezera. Davide anayesa kupeza njira yoti tchimo lakelo lisadziwike. Iye anauza mkulu wa asilikali kuti aike Uriya kutsogolo n’kumusiya kuti aphedwe. Uriya ataphedwa ku nkhondo, Davide anakwatira Bati-seba.

Mfumu Davide akupempha Mulungu kuti amukhululukire

Koma Yehova ankaona zoipa zonsezi. Ndiye kodi anatani? Iye anatumiza Natani kuti akakambirane ndi Davide za nkhaniyi. Natani atafika kwa Davide anamuuza kuti: ‘Panali munthu wina wolemera amene anali ndi nkhosa zambiri ndiye panalinso wosauka yemwe anali ndi kankhosa kamodzi kokha. Wosaukayo ankakakonda kwambiri kankhosa kakeko. Ndiyeno munthu wolemera uja analanda kankhosa ka wosaukayo kuti kakhalenso kake.’ Davide atamva zimenezi, anakwiya kwambiri ndipo anati: ‘Munthu ameneyu ayenera kufa basi.’ Natani anauza Davide kuti: ‘Munthu wolemerayo ndi inuyo.’ Davide anazindikira zimene Natani ankatanthauza ndipo anamva chisoni. Ndiyeno anauza Natani kuti: ‘Ndachimwira Yehova.’ Tchimo limeneli linam’bweretsera mavuto Davide limodzi ndi banja lake. Yehova anapereka chilango kwa Davide koma sanamuphe chifukwa anadzichepetsa komanso analapa kuchokera pansi pa mtima.

Davide ankafuna kumanga nyumba ya Yehova. Koma Yehova anasankha mwana wake Solomo kuti ndi amene adzamange nyumbayo. Davide anayamba kusonkhanitsa zinthu zoti Solomo adzagwiritse ntchito pomanga. Iye anati: ‘Nyumba ya Yehova ikufunika idzakhale yokongola kwambiri. Popeza Solomo adakali mwana, ndimuthandiza kupeza zipangizo zomangira nyumbayi.’ Choncho Davide anapereka ndalama zambiri zoti zidzathandize pa ntchito yomanga nyumbayo. Anapeza anthu aluso komanso anasonkhanitsa golide ndi siliva wambiri ndiponso anasonkhanitsa matabwa a mtengo wa mkungudza ochokera ku Turo ndi ku Sidoni. Davide atatsala pang’ono kumwalira, anapatsa Solomo pulani ya mmene adzamangire nyumbayo. Anati: ‘Yehova anandiuza kuti ndikulembere pulaniyi. Usachite mantha chifukwa iye akuthandiza. Limba mtima ndipo yamba kugwira ntchitoyi.’

Davide akukambirana ndi Solomo zokhudza mapulani a kachisi

“Wobisa machimo ake zinthu sizidzamuyendera bwino, koma amene amawaulula nʼkuwasiya adzachitiridwa chifundo.”​—Miyambo 28:13

Mafunso: Kodi Davide anachita tchimo lotani? Kodi Davide anathandiza bwanji Solomo kuti amange nyumba ya Yehova?

2 Samueli 5:3, 4, 10; 7:1-16; 8:1-14; 11:1-27; 12:1-14; 1 Mbiri 22:1-19; 28:11-21; Salimo 51:1-19

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena